< Masalimo 99 >

1 Yehova akulamulira, mitundu ya anthu injenjemere; Iye wakhala pa mpando wake waufumu, pakati pa akerubi, dziko lapansi ligwedezeke.
¡Yavé reina! ¡Tiemblen los pueblos! Él mora entre los querubines. ¡Que se conmueva la tierra!
2 Mʼziyoni wamkulu ndi Yehova; Iye ndi wokwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.
Yavé es grande en Sion, Y Él es exaltado sobre todos los pueblos.
3 Anthu atamande dzina lanu lalikulu ndi loopsa kwambiri, Iye ndi woyera.
Que alaben tu grande y asombroso Nombre. ¡Santo es Él!
4 Mfumu yamphamvu, iyo imakonda chilungamo Inu mwakhazikitsa khalidwe losakondera; mwachita zolungama ndi zoyenera mwa Yakobo.
La fuerza del Rey ama la justicia. Tú has ejecutado equidad y justicia en Jacob.
5 Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mulambireni pa mapazi ake; Iye ndi woyera.
Exalten a Yavé nuestro ʼElohim, Y póstrense ante el estrado de sus pies, ¡Santo es Él!
6 Mose ndi Aaroni anali ena mwa ansembe ake, Samueli anali pamodzi ndi iwo amene anayitana pa dzina lake; iwo anayitana Yehova ndipo Iyeyo anawayankha.
Moisés y Aarón estuvieron entre sus sacerdotes, Y Samuel estuvo entre los que invocaron su Nombre. Invocaban a Yavé, y Él les respondía.
7 Iye anayankhula nawo kuchokera mʼchipilala cha mtambo; iwo anasunga malamulo ake ndi zophunzitsa zomwe anawapatsa.
En la columna de nube hablaba con ellos. Ellos guardaron sus Testimonios y el estatuto que Él les dio.
8 Inu Yehova Mulungu wathu, munawayankha iwo; Inu kwa Israeli munali Mulungu wokhululuka, ngakhale munawalanga pa zochita zawo zoyipa.
Oh Yavé, ʼElohim nuestro, Tú les respondías. Fuiste para ellos un ʼEL perdonador, Aunque vindicador de sus [malas] obras.
9 Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mumulambire pa phiri lake loyera, pakuti Yehova Mulungu wathu ndi woyera.
Exalten a Yavé nuestro ʼElohim Y póstrense hacia su Montaña Santa, Porque Yavé nuestro ʼElohim es santo.

< Masalimo 99 >