< Masalimo 99 >

1 Yehova akulamulira, mitundu ya anthu injenjemere; Iye wakhala pa mpando wake waufumu, pakati pa akerubi, dziko lapansi ligwedezeke.
Gospod caruje: neka strepe narodi; sjedi na heruvimima: nek se drma zemlja!
2 Mʼziyoni wamkulu ndi Yehova; Iye ndi wokwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.
Gospod je na Sionu velik, i visok nad svima narodima.
3 Anthu atamande dzina lanu lalikulu ndi loopsa kwambiri, Iye ndi woyera.
Neka slave veliko i strašno ime tvoje; da je svet!
4 Mfumu yamphamvu, iyo imakonda chilungamo Inu mwakhazikitsa khalidwe losakondera; mwachita zolungama ndi zoyenera mwa Yakobo.
Neka slave silu cara koji ljubi pravdu. Ti si utvrdio pravdu; sud i pravdu ti si uredio u Jakovu.
5 Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mulambireni pa mapazi ake; Iye ndi woyera.
Uzvišujte Gospoda Boga našega, i klanjajte se podnožju njegovu; da je svet!
6 Mose ndi Aaroni anali ena mwa ansembe ake, Samueli anali pamodzi ndi iwo amene anayitana pa dzina lake; iwo anayitana Yehova ndipo Iyeyo anawayankha.
Mojsije i Aron, sveštenici njegovi, i Samuilo jedan od onijeh koji prizivlju ime njegovo, prizivahu Boga, i on ih usliši.
7 Iye anayankhula nawo kuchokera mʼchipilala cha mtambo; iwo anasunga malamulo ake ndi zophunzitsa zomwe anawapatsa.
U stupu od oblaka govoraše njima; oni èuvaše zapovijesti njegove i uredbu koju im dade.
8 Inu Yehova Mulungu wathu, munawayankha iwo; Inu kwa Israeli munali Mulungu wokhululuka, ngakhale munawalanga pa zochita zawo zoyipa.
Gospode, Bože naš, ti si ih uslišio; ti si im bio Bog blag i plaæao za djela njihova.
9 Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mumulambire pa phiri lake loyera, pakuti Yehova Mulungu wathu ndi woyera.
Uzvišujte Gospoda Boga našega, i klanjajte se na svetoj gori njegovoj, jer je svet Gospod Bog naš.

< Masalimo 99 >