< Masalimo 99 >
1 Yehova akulamulira, mitundu ya anthu injenjemere; Iye wakhala pa mpando wake waufumu, pakati pa akerubi, dziko lapansi ligwedezeke.
Pan króluje, niechże zadrżą narody; siedzi między Cherubinami, niechże się poruszy ziemia.
2 Mʼziyoni wamkulu ndi Yehova; Iye ndi wokwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.
Pan na Syonie wielki, a wywyższony nad wszystkie narody.
3 Anthu atamande dzina lanu lalikulu ndi loopsa kwambiri, Iye ndi woyera.
Niech wysławiają imię twoje wielkie i straszne; albowiem święte jest.
4 Mfumu yamphamvu, iyo imakonda chilungamo Inu mwakhazikitsa khalidwe losakondera; mwachita zolungama ndi zoyenera mwa Yakobo.
Moc zaiste królewska miłuje sąd; albowiemeś ty ustanowił prawa; sąd i sprawiedliwość w Jakóbie ty wykonujesz.
5 Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mulambireni pa mapazi ake; Iye ndi woyera.
Wywyższajcie Pana, Boga naszego, a kłaniajcie się u podnóżka nóg jego; bo święty jest.
6 Mose ndi Aaroni anali ena mwa ansembe ake, Samueli anali pamodzi ndi iwo amene anayitana pa dzina lake; iwo anayitana Yehova ndipo Iyeyo anawayankha.
Mojżesz i Aaron między kapłanami jego, a Samuel między wzywającymi imienia jego, wołali do Pana, a on ich wysłuchał.
7 Iye anayankhula nawo kuchokera mʼchipilala cha mtambo; iwo anasunga malamulo ake ndi zophunzitsa zomwe anawapatsa.
W słupie obłokowym mówił do nich; a gdy strzegli świadectw jego i ustaw, które im podał,
8 Inu Yehova Mulungu wathu, munawayankha iwo; Inu kwa Israeli munali Mulungu wokhululuka, ngakhale munawalanga pa zochita zawo zoyipa.
Panie, Boże nasz! tyś ich wysłuchiwał; Boże! bywałeś im miłościwym, i gdyś ich karał dla występków ich.
9 Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mumulambire pa phiri lake loyera, pakuti Yehova Mulungu wathu ndi woyera.
Wywyższajcie Pana, Boga naszego, a kłaniajcie się na górze świętej jego; albowiem święty jest Pan, Bóg nasz.