< Masalimo 99 >

1 Yehova akulamulira, mitundu ya anthu injenjemere; Iye wakhala pa mpando wake waufumu, pakati pa akerubi, dziko lapansi ligwedezeke.
L'Éternel règne, les peuples tremblent; Il est assis sur les Chérubins, la terre est ébranlée.
2 Mʼziyoni wamkulu ndi Yehova; Iye ndi wokwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.
L'Éternel est grand en Sion, et élevé au-dessus de tous les peuples:
3 Anthu atamande dzina lanu lalikulu ndi loopsa kwambiri, Iye ndi woyera.
qu'ils chantent Ton nom grand et redoutable, Il est saint!
4 Mfumu yamphamvu, iyo imakonda chilungamo Inu mwakhazikitsa khalidwe losakondera; mwachita zolungama ndi zoyenera mwa Yakobo.
et la force du Roi qui aime la justice! Tu as fondé l'équité, et créé en Jacob la justice et le droit.
5 Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mulambireni pa mapazi ake; Iye ndi woyera.
Exaltez l'Éternel, notre Dieu, et vous prosternez sur le marchepied de son trône! Il est saint!
6 Mose ndi Aaroni anali ena mwa ansembe ake, Samueli anali pamodzi ndi iwo amene anayitana pa dzina lake; iwo anayitana Yehova ndipo Iyeyo anawayankha.
Moïse et Aaron, ses Lévites, et Samuel qui invoquait son nom, implorèrent l'Éternel, et Il les exauça.
7 Iye anayankhula nawo kuchokera mʼchipilala cha mtambo; iwo anasunga malamulo ake ndi zophunzitsa zomwe anawapatsa.
Il leur parla dans la colonne de nuée; ils gardèrent ses commandements, et l'ordonnance qu'il leur avait donnée.
8 Inu Yehova Mulungu wathu, munawayankha iwo; Inu kwa Israeli munali Mulungu wokhululuka, ngakhale munawalanga pa zochita zawo zoyipa.
Éternel, notre Dieu, tu les as exaucés; tu fus pour eux un Dieu qui pardonne, et un Dieu vengeur, à cause de leurs méfaits.
9 Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mumulambire pa phiri lake loyera, pakuti Yehova Mulungu wathu ndi woyera.
Exaltez l'Éternel, notre Dieu, et prosternez-vous sur sa sainte montagne! Car Il est saint, l'Éternel, notre Dieu.

< Masalimo 99 >