< Masalimo 99 >

1 Yehova akulamulira, mitundu ya anthu injenjemere; Iye wakhala pa mpando wake waufumu, pakati pa akerubi, dziko lapansi ligwedezeke.
The Lord hath regned, puplis ben wrooth; thou that sittist on cherubyn, the erthe be moued.
2 Mʼziyoni wamkulu ndi Yehova; Iye ndi wokwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.
The Lord is greet in Sion; and hiy aboue alle puplis.
3 Anthu atamande dzina lanu lalikulu ndi loopsa kwambiri, Iye ndi woyera.
Knouleche thei to thi greet name, for it is ferdful and hooli;
4 Mfumu yamphamvu, iyo imakonda chilungamo Inu mwakhazikitsa khalidwe losakondera; mwachita zolungama ndi zoyenera mwa Yakobo.
and the onour of the king loueth doom. Thou hast maad redi dressyngis; thou hast maad doom and riytfulnesse in Jacob.
5 Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mulambireni pa mapazi ake; Iye ndi woyera.
Enhaunse ye oure Lord God; and worschipe ye the stool of hise feet, for it is hooli.
6 Mose ndi Aaroni anali ena mwa ansembe ake, Samueli anali pamodzi ndi iwo amene anayitana pa dzina lake; iwo anayitana Yehova ndipo Iyeyo anawayankha.
Moises and Aaron weren among hise preestis; and Samuel was among hem that inwardli clepen his name. Thei inwardli clepiden the Lord, and he herde hem;
7 Iye anayankhula nawo kuchokera mʼchipilala cha mtambo; iwo anasunga malamulo ake ndi zophunzitsa zomwe anawapatsa.
in a piler of cloude he spak to hem. Thei kepten hise witnessyngis; and the comaundement which he yaf to hem.
8 Inu Yehova Mulungu wathu, munawayankha iwo; Inu kwa Israeli munali Mulungu wokhululuka, ngakhale munawalanga pa zochita zawo zoyipa.
Oure Lord God, thou herdist hem; God, thou were merciful to hem, and thou tokist veniaunce on al her fyndyngis.
9 Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mumulambire pa phiri lake loyera, pakuti Yehova Mulungu wathu ndi woyera.
Enhaunse ye oure Lord God, and worschipe ye in his hooli hil; for oure Lord God is hooli.

< Masalimo 99 >