< Masalimo 99 >

1 Yehova akulamulira, mitundu ya anthu injenjemere; Iye wakhala pa mpando wake waufumu, pakati pa akerubi, dziko lapansi ligwedezeke.
Jehovah reigns! Let the peoples tremble. He sits above the cherubim, let the earth be moved.
2 Mʼziyoni wamkulu ndi Yehova; Iye ndi wokwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.
Jehovah is great in Zion, and he is high above all the peoples.
3 Anthu atamande dzina lanu lalikulu ndi loopsa kwambiri, Iye ndi woyera.
Let them praise thy great and awesome name. Holy is he.
4 Mfumu yamphamvu, iyo imakonda chilungamo Inu mwakhazikitsa khalidwe losakondera; mwachita zolungama ndi zoyenera mwa Yakobo.
The king's strength also loves justice. Thou establish equity. Thou execute justice and righteousness in Jacob.
5 Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mulambireni pa mapazi ake; Iye ndi woyera.
Exalt ye Jehovah our God, and worship at his footstool. Holy is he.
6 Mose ndi Aaroni anali ena mwa ansembe ake, Samueli anali pamodzi ndi iwo amene anayitana pa dzina lake; iwo anayitana Yehova ndipo Iyeyo anawayankha.
Moses and Aaron among his priests, and Samuel among those who call upon his name, they called upon Jehovah, and he answered them.
7 Iye anayankhula nawo kuchokera mʼchipilala cha mtambo; iwo anasunga malamulo ake ndi zophunzitsa zomwe anawapatsa.
He spoke to them in the pillar of cloud. They kept his testimonies, and the statute that he gave them.
8 Inu Yehova Mulungu wathu, munawayankha iwo; Inu kwa Israeli munali Mulungu wokhululuka, ngakhale munawalanga pa zochita zawo zoyipa.
Thou answered them, O Jehovah our God. Thou were a God who forgave them, though thou took vengeance on their doings.
9 Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mumulambire pa phiri lake loyera, pakuti Yehova Mulungu wathu ndi woyera.
Exalt ye Jehovah our God, and worship at his holy hill. For Jehovah our God is holy.

< Masalimo 99 >