< Masalimo 99 >

1 Yehova akulamulira, mitundu ya anthu injenjemere; Iye wakhala pa mpando wake waufumu, pakati pa akerubi, dziko lapansi ligwedezeke.
Herren regerer, Folkene bæve; han sidder over Keruber, Jorden ryster.
2 Mʼziyoni wamkulu ndi Yehova; Iye ndi wokwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.
Herren er stor i Zion, og han er ophøjet over alle Folkene.
3 Anthu atamande dzina lanu lalikulu ndi loopsa kwambiri, Iye ndi woyera.
De skulle prise dit Navn som stort og forfærdeligt — hellig er han! —
4 Mfumu yamphamvu, iyo imakonda chilungamo Inu mwakhazikitsa khalidwe losakondera; mwachita zolungama ndi zoyenera mwa Yakobo.
Og Kongens Vælde elsker Ret; du har befæstet Retvished, du har gjort Ret og Retfærdighed i Jakob.
5 Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mulambireni pa mapazi ake; Iye ndi woyera.
Ophøjer Herren vor Gud og tilbeder for hans Fødders Fodskammel — hellig er han! —
6 Mose ndi Aaroni anali ena mwa ansembe ake, Samueli anali pamodzi ndi iwo amene anayitana pa dzina lake; iwo anayitana Yehova ndipo Iyeyo anawayankha.
Mose og Aron iblandt hans Præster og Samuel iblandt dem, som paakaldte hans Navn, raabte til Herren, og han bønhørte dem.
7 Iye anayankhula nawo kuchokera mʼchipilala cha mtambo; iwo anasunga malamulo ake ndi zophunzitsa zomwe anawapatsa.
Han talte til dem i Skystøtten; de holdt hans Vidnesbyrd og den Skik, som han gav dem.
8 Inu Yehova Mulungu wathu, munawayankha iwo; Inu kwa Israeli munali Mulungu wokhululuka, ngakhale munawalanga pa zochita zawo zoyipa.
Herre, vor Gud! du bønhørte dem, du var dem en Gud, som tilgav dem, men ogsaa en Hævner over deres Gerninger.
9 Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mumulambire pa phiri lake loyera, pakuti Yehova Mulungu wathu ndi woyera.
Ophøjer Herren vor Gud og tilbeder for hans hellige Bjerg; thi hellig er Herren vor Gud.

< Masalimo 99 >