< Masalimo 99 >
1 Yehova akulamulira, mitundu ya anthu injenjemere; Iye wakhala pa mpando wake waufumu, pakati pa akerubi, dziko lapansi ligwedezeke.
Jahve kraljuje - nek' zadršću narodi; sjedi nad kerubima - zemlja nek' se potrese!
2 Mʼziyoni wamkulu ndi Yehova; Iye ndi wokwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.
Velik je Jahve na Sionu, uzvišen nada sve narode.
3 Anthu atamande dzina lanu lalikulu ndi loopsa kwambiri, Iye ndi woyera.
Nek' slave ime tvoje veliko i strašno: ono je sveto!
4 Mfumu yamphamvu, iyo imakonda chilungamo Inu mwakhazikitsa khalidwe losakondera; mwachita zolungama ndi zoyenera mwa Yakobo.
Ti kralj si moćan koji ljubiš što je pravo, pravednost ti si utvrdio, pravo i pravednost vršiš u Jakovu.
5 Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mulambireni pa mapazi ake; Iye ndi woyera.
Uzvisujte Jahvu, Boga našega, padnite pred podnožje njegovo: ono je sveto.
6 Mose ndi Aaroni anali ena mwa ansembe ake, Samueli anali pamodzi ndi iwo amene anayitana pa dzina lake; iwo anayitana Yehova ndipo Iyeyo anawayankha.
Mojsije i Aron među svećenicima njegovim i Samuel među onima koji zazivaju ime njegovo: zazivahu Jahvu, i on ih usliša.
7 Iye anayankhula nawo kuchokera mʼchipilala cha mtambo; iwo anasunga malamulo ake ndi zophunzitsa zomwe anawapatsa.
Iz stupa od oblaka govoraše njima: slušahu zapovijedi njegove i odredbe što ih dade.
8 Inu Yehova Mulungu wathu, munawayankha iwo; Inu kwa Israeli munali Mulungu wokhululuka, ngakhale munawalanga pa zochita zawo zoyipa.
Jahve, Bože naš, ti si ih uslišivao; Bože, milostiv si bio njima premda si kažnjavao grijehe njihove.
9 Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mumulambire pa phiri lake loyera, pakuti Yehova Mulungu wathu ndi woyera.
Uzvisujte Jahvu, Boga našega, padnite pred svetu goru njegovu: jer svet je Jahve, Bog naš.