< Masalimo 98 >
1 Salimo. Imbirani Yehova nyimbo yatsopano, pakuti Iyeyo wachita zinthu zodabwitsa; dzanja lake lamanja ndi mkono wake woyera zamuchitira chipulumutso.
Псалом. Співайте Господеві нову пісню, бо Він здійснив чудеса; перемогу принесла Йому правиця Його і рамено Його святе.
2 Yehova waonetsa chipulumutso chake ndipo waulula chilungamo chake kwa anthu a mitundu ina.
Звістив Господь спасіння Своє, відкрив перед очима народів праведність Свою.
3 Iye wakumbukira chikondi chake ndi kukhulupirika kwake pa Aisraeli; malekezero onse a dziko lapansi aona chipulumutso cha Mulungu wathu.
Згадав Він милість Свою й вірність Свою дому Ізраїля. Усі краї землі побачили спасіння Бога нашого.
4 Fuwulani mwachimwemwe kwa Yehova, dziko lonse lapansi, muyimbireni nyimbo mofuwula ndi mokondwera.
Вигукни радісно Господеві, уся земле! Кричи від радості, веселися й співай!
5 Imbirani Yehova nyimbo ndi zeze, ndi zeze ndi mawu a kuyimba,
Грайте Господеві на арфі, на арфі зі звуками співу!
6 ndi malipenga ndi kuliza kwa nyanga ya nkhosa yayimuna fuwulani mwachimwemwe pamaso pa Yehova Mfumu.
Під звуки труб і сурми вигукуйте радісно перед Царем, Господом!
7 Nyanja ikokome pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo, dziko lonse ndi onse amene amakhala mʼmenemo.
Нехай гуркотить море і все, що його наповнює, всесвіт і все, що мешкає в ньому.
8 Mitsinje iwombe mʼmanja mwawo, mapiri ayimbe pamodzi mwachimwemwe;
Нехай ріки плещуть у долоні, нехай гори веселяться разом
9 izo ziyimbe pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi. Adzaweruza dziko lonse mwachilungamo, ndi mitundu ya anthu mosakondera.
перед обличчям Господа, бо Він іде судити землю. Він судитиме всесвіт праведно й народи – справедливо.