< Masalimo 98 >
1 Salimo. Imbirani Yehova nyimbo yatsopano, pakuti Iyeyo wachita zinthu zodabwitsa; dzanja lake lamanja ndi mkono wake woyera zamuchitira chipulumutso.
Psaume. Chantez à l'Éternel un cantique nouveau! Car il a fait des choses merveilleuses; sa droite et le bras de sa sainteté l'ont délivré.
2 Yehova waonetsa chipulumutso chake ndipo waulula chilungamo chake kwa anthu a mitundu ina.
L'Éternel a fait connaître son salut; il a révélé sa justice aux yeux des nations.
3 Iye wakumbukira chikondi chake ndi kukhulupirika kwake pa Aisraeli; malekezero onse a dziko lapansi aona chipulumutso cha Mulungu wathu.
Il s'est souvenu de sa bonté et de sa fidélité envers la maison d'Israël; tous les bouts de la terre ont vu le salut de notre Dieu.
4 Fuwulani mwachimwemwe kwa Yehova, dziko lonse lapansi, muyimbireni nyimbo mofuwula ndi mokondwera.
Vous, toute la terre, jetez des cris de réjouissance à l'Éternel; éclatez en cris de joie, et chantez!
5 Imbirani Yehova nyimbo ndi zeze, ndi zeze ndi mawu a kuyimba,
Chantez à l'Éternel avec la harpe, avec la harpe et la voix des cantiques!
6 ndi malipenga ndi kuliza kwa nyanga ya nkhosa yayimuna fuwulani mwachimwemwe pamaso pa Yehova Mfumu.
Avec les cors et le son des trompettes, poussez des cris de joie, devant le Roi, l'Éternel!
7 Nyanja ikokome pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo, dziko lonse ndi onse amene amakhala mʼmenemo.
Que la mer retentisse, avec tout ce qu'elle contient; le monde, avec ceux qui l'habitent!
8 Mitsinje iwombe mʼmanja mwawo, mapiri ayimbe pamodzi mwachimwemwe;
Que les fleuves battent des mains, que toutes les montagnes chantent de joie, devant l'Éternel!
9 izo ziyimbe pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi. Adzaweruza dziko lonse mwachilungamo, ndi mitundu ya anthu mosakondera.
Car il vient pour juger la terre; il jugera le monde avec justice, et les peuples avec équité.