< Masalimo 98 >
1 Salimo. Imbirani Yehova nyimbo yatsopano, pakuti Iyeyo wachita zinthu zodabwitsa; dzanja lake lamanja ndi mkono wake woyera zamuchitira chipulumutso.
A Psalm. O sing to the LORD a new song; for he hath done marvellous things: his right hand, and his holy arm, hath gotten him the victory.
2 Yehova waonetsa chipulumutso chake ndipo waulula chilungamo chake kwa anthu a mitundu ina.
The LORD hath made known his salvation: his righteousness hath he openly shown in the sight of the heathen.
3 Iye wakumbukira chikondi chake ndi kukhulupirika kwake pa Aisraeli; malekezero onse a dziko lapansi aona chipulumutso cha Mulungu wathu.
He hath remembered his mercy and his truth toward the house of Israel: all the ends of the earth have seen the salvation of our God.
4 Fuwulani mwachimwemwe kwa Yehova, dziko lonse lapansi, muyimbireni nyimbo mofuwula ndi mokondwera.
Make a joyful noise to the LORD, all the earth: make a loud noise, and rejoice, and sing praise.
5 Imbirani Yehova nyimbo ndi zeze, ndi zeze ndi mawu a kuyimba,
Sing to the LORD with the harp; with the harp, and the voice of a psalm.
6 ndi malipenga ndi kuliza kwa nyanga ya nkhosa yayimuna fuwulani mwachimwemwe pamaso pa Yehova Mfumu.
With trumpets and sound of cornet make a joyful noise before the LORD, the King.
7 Nyanja ikokome pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo, dziko lonse ndi onse amene amakhala mʼmenemo.
Let the sea roar, and all it containeth; the world, and they that dwell in it.
8 Mitsinje iwombe mʼmanja mwawo, mapiri ayimbe pamodzi mwachimwemwe;
Let the floods clap their hands: let the hills be joyful together
9 izo ziyimbe pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi. Adzaweruza dziko lonse mwachilungamo, ndi mitundu ya anthu mosakondera.
Before the LORD; for he cometh to judge the earth: with righteousness shall he judge the world, and the people with equity.