< Masalimo 98 >
1 Salimo. Imbirani Yehova nyimbo yatsopano, pakuti Iyeyo wachita zinthu zodabwitsa; dzanja lake lamanja ndi mkono wake woyera zamuchitira chipulumutso.
A psalm. Oh, sing to Yahweh a new song, for he has done marvelous things; his right hand and his holy arm have given him victory.
2 Yehova waonetsa chipulumutso chake ndipo waulula chilungamo chake kwa anthu a mitundu ina.
Yahweh has made known his salvation; he has openly showed his justice to all the nations.
3 Iye wakumbukira chikondi chake ndi kukhulupirika kwake pa Aisraeli; malekezero onse a dziko lapansi aona chipulumutso cha Mulungu wathu.
He calls to mind his covenant loyalty and faithfulness for the house of Israel; all the ends of the earth will see the victory of our God.
4 Fuwulani mwachimwemwe kwa Yehova, dziko lonse lapansi, muyimbireni nyimbo mofuwula ndi mokondwera.
Shout for joy to Yahweh, all the earth; burst into song, sing for joy, and sing praises.
5 Imbirani Yehova nyimbo ndi zeze, ndi zeze ndi mawu a kuyimba,
Sing praises to Yahweh with the harp, with the harp and melodious song.
6 ndi malipenga ndi kuliza kwa nyanga ya nkhosa yayimuna fuwulani mwachimwemwe pamaso pa Yehova Mfumu.
With trumpets and the sound of the horn, make a joyful noise before the King, Yahweh.
7 Nyanja ikokome pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo, dziko lonse ndi onse amene amakhala mʼmenemo.
Let the sea shout and everything in it, the world and those who live in it!
8 Mitsinje iwombe mʼmanja mwawo, mapiri ayimbe pamodzi mwachimwemwe;
Let the rivers clap their hands, and let the mountains shout for joy.
9 izo ziyimbe pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi. Adzaweruza dziko lonse mwachilungamo, ndi mitundu ya anthu mosakondera.
Yahweh is coming to judge the earth; he will judge the world with righteousness and the nations with fairness.