< Masalimo 98 >

1 Salimo. Imbirani Yehova nyimbo yatsopano, pakuti Iyeyo wachita zinthu zodabwitsa; dzanja lake lamanja ndi mkono wake woyera zamuchitira chipulumutso.
A psalm for David himself. Sing ye to the Lord anew canticle: because he hath done wonderful things. His right hand hath wrought for him salvation, and his arm is holy.
2 Yehova waonetsa chipulumutso chake ndipo waulula chilungamo chake kwa anthu a mitundu ina.
The Lord hath made known his salvation: he hath revealed his justice in the sight of the Gentiles.
3 Iye wakumbukira chikondi chake ndi kukhulupirika kwake pa Aisraeli; malekezero onse a dziko lapansi aona chipulumutso cha Mulungu wathu.
He hath remembered his mercy his truth toward the house of Israel. All the ends of the earth have seen the salvation of our God.
4 Fuwulani mwachimwemwe kwa Yehova, dziko lonse lapansi, muyimbireni nyimbo mofuwula ndi mokondwera.
Sing joyfully to God, all the earth; make melody, rejoice and sing.
5 Imbirani Yehova nyimbo ndi zeze, ndi zeze ndi mawu a kuyimba,
Sing praise to the Lord on the harp, on the harp, and with the voice of a psalm:
6 ndi malipenga ndi kuliza kwa nyanga ya nkhosa yayimuna fuwulani mwachimwemwe pamaso pa Yehova Mfumu.
With long trumpets, and sound of comet. Make a joyful noise before the Lord our king:
7 Nyanja ikokome pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo, dziko lonse ndi onse amene amakhala mʼmenemo.
Let the sea be moved and the fulness thereof: the world and they that dwell therein.
8 Mitsinje iwombe mʼmanja mwawo, mapiri ayimbe pamodzi mwachimwemwe;
The rivers shall clap their hands, the mountains shall rejoice together
9 izo ziyimbe pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi. Adzaweruza dziko lonse mwachilungamo, ndi mitundu ya anthu mosakondera.
At the presence of the Lord: because he cometh to judge the earth. He shall judge the world with justice, and the people with equity.

< Masalimo 98 >