< Masalimo 98 >

1 Salimo. Imbirani Yehova nyimbo yatsopano, pakuti Iyeyo wachita zinthu zodabwitsa; dzanja lake lamanja ndi mkono wake woyera zamuchitira chipulumutso.
(En Salme.) Syng HERREN en sang, thi vidunderlige ting har han gjort; Sejren vandt ham hans højre, hans hellige Arm.
2 Yehova waonetsa chipulumutso chake ndipo waulula chilungamo chake kwa anthu a mitundu ina.
Sin Frelse har HERREN gjort kendt, åbenbaret sin Retfærd for Folkenes Øjne;
3 Iye wakumbukira chikondi chake ndi kukhulupirika kwake pa Aisraeli; malekezero onse a dziko lapansi aona chipulumutso cha Mulungu wathu.
han kom sin Nåde mod Jakob i Hu, sin Trofasthed mod Israels Hus. Den vide Jord har skuet vor Guds Frelse.
4 Fuwulani mwachimwemwe kwa Yehova, dziko lonse lapansi, muyimbireni nyimbo mofuwula ndi mokondwera.
Råb af Fryd for HERREN, al Jorden, bryd ud i Jubel og Lovsang;
5 Imbirani Yehova nyimbo ndi zeze, ndi zeze ndi mawu a kuyimba,
lovsyng HERREN til Citer, lad Lovsang tone til Citer,
6 ndi malipenga ndi kuliza kwa nyanga ya nkhosa yayimuna fuwulani mwachimwemwe pamaso pa Yehova Mfumu.
råb af Fryd for Kongen, HERREN, til Trompeter og Hornets Klang!
7 Nyanja ikokome pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo, dziko lonse ndi onse amene amakhala mʼmenemo.
Havet med dets Fylde skal bruse, Jorderig og de, som bor der,
8 Mitsinje iwombe mʼmanja mwawo, mapiri ayimbe pamodzi mwachimwemwe;
Strømmene klappe i Hænder, Bjergene juble til Hobe
9 izo ziyimbe pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi. Adzaweruza dziko lonse mwachilungamo, ndi mitundu ya anthu mosakondera.
for HERRENs Åsyn, thi han kommer, han kommer at dømme Jorden; han dømmer Jorden med Retfærd og Folkeslag med Ret!

< Masalimo 98 >