< Masalimo 98 >
1 Salimo. Imbirani Yehova nyimbo yatsopano, pakuti Iyeyo wachita zinthu zodabwitsa; dzanja lake lamanja ndi mkono wake woyera zamuchitira chipulumutso.
Žalm. Zpívejte Hospodinu píseň novou, neboť jest divné věci učinil; spomohla mu pravice jeho, a rámě svatosti jeho.
2 Yehova waonetsa chipulumutso chake ndipo waulula chilungamo chake kwa anthu a mitundu ina.
V známost uvedl Hospodin spasení své, před očima národů zjevil spravedlnost svou.
3 Iye wakumbukira chikondi chake ndi kukhulupirika kwake pa Aisraeli; malekezero onse a dziko lapansi aona chipulumutso cha Mulungu wathu.
Rozpomenul se na milosrdenství své, a na pravdu svou k domu Izraelskému; všecky končiny země vidí spasení Boha našeho.
4 Fuwulani mwachimwemwe kwa Yehova, dziko lonse lapansi, muyimbireni nyimbo mofuwula ndi mokondwera.
Prokřikuj Hospodinu všecka země; zvuk vydejte, prozpěvujte, a žalmy zpívejte.
5 Imbirani Yehova nyimbo ndi zeze, ndi zeze ndi mawu a kuyimba,
Žalmy zpívejte Hospodinu na citaře, k citaře i hlasem přizpěvujte.
6 ndi malipenga ndi kuliza kwa nyanga ya nkhosa yayimuna fuwulani mwachimwemwe pamaso pa Yehova Mfumu.
Trubami a zvučnými pozouny hlas vydejte před králem Hospodinem.
7 Nyanja ikokome pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo, dziko lonse ndi onse amene amakhala mʼmenemo.
Zvuč moře i to, což v něm jest, okršlek světa i ti, kteříž na něm bydlí.
8 Mitsinje iwombe mʼmanja mwawo, mapiri ayimbe pamodzi mwachimwemwe;
Řeky rukama plésejte, spolu i hory prozpěvujte,
9 izo ziyimbe pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi. Adzaweruza dziko lonse mwachilungamo, ndi mitundu ya anthu mosakondera.
Před Hospodinem; neboť se béře, aby soudil zemi. Budeť souditi okršlek světa v spravedlnosti, a národy v pravosti.