< Masalimo 97 >
1 Yehova akulamulira, dziko lapansi lisangalale; magombe akutali akondwere.
Herren er konge; jordi fagne seg, mange øyar glede seg!
2 Mitambo ndi mdima waukulu zamuzungulira; chilungamo ndi kuweruza molungama ndiwo maziko a mpando wake waufumu.
Skyer og myrker er kringum honom, rettferd og rett er grunnvoll for hans kongsstol.
3 Moto umapita patsogolo pake ndi kunyeketsa amaliwongo kumbali zonse.
Eld gjeng framfyre honom og brenner hans motstandarar rundt ikring.
4 Zingʼaningʼani zake zimawalitsa dziko lonse; dziko lapansi limaona ndipo limanjenjemera.
Hans eldingar lyser upp heimen; jordi ser det og skjelv.
5 Mapiri amasungunuka ngati phula pamaso pa Yehova, pamaso pa Ambuye a dziko lonse lapansi.
Bergi brånar som voks for Herren, for Herren yver all jordi.
6 Mayiko akumwamba amalengeza za chilungamo chake, ndipo mitundu yonse ya anthu imaona ulemerero wake.
Himmelen forkynner hans rettferd, og alle folki hans æra.
7 Onse amene amalambira mafano osema amachititsidwa manyazi, iwo amene amanyadira mafano; mulambireni, inu milungu yonse!
Skjemde vert alle som dyrkar bilæte, som rosar seg av avgudar. Alle gudar tilbed honom.
8 Ziyoni akumva ndipo akukondwera, midzi ya Yuda ikusangalala chifukwa cha maweruzo anu Yehova.
Sion høyrer det og gled seg, og Judas døtter fagnar seg for dine domar skuld, Herre.
9 Pakuti Inu Yehova ndi Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi; ndinu wokwezeka kupambana milungu yonse.
For du, Herre, er den høgste yver heile jordi, du er høgt upphøgd yver alle gudar.
10 Iwo amene amakonda Yehova adane ndi zoyipa pakuti Iye amayangʼanira miyoyo ya amene amamukhulupirira ndipo amawapulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa
De som elskar Herren, hata det vonde! Han tek vare på sjælerne åt sine trugne, frå handi til dei ugudlege frelsar han deim.
11 Kuwala kumafika pa anthu olungama, ndi chimwemwe kwa olungama mtima.
Ljos er utsått for den rettferdige, og gleda for dei ærlege i hjarta.
12 Kondwerani mwa Yehova Inu olungama ndipo tamandani dzina lake loyera.
Gled dykk, de rettferdige, i Herren! Syng lov for hans heilage namn!