< Masalimo 97 >

1 Yehova akulamulira, dziko lapansi lisangalale; magombe akutali akondwere.
UThixo uyabusa, umhlaba kawuthokoze; akuthi amakhumbi akude ajabule.
2 Mitambo ndi mdima waukulu zamuzungulira; chilungamo ndi kuweruza molungama ndiwo maziko a mpando wake waufumu.
Amayezi lomnyama omkhulu kumsibekele; ukulunga lokwahlulela kuhle kuyisisekelo sesihlalo Sakhe sobukhosi.
3 Moto umapita patsogolo pake ndi kunyeketsa amaliwongo kumbali zonse.
Umlilo uhamba phambi Kwakhe uzihangule izitha zakhe inxa zonke.
4 Zingʼaningʼani zake zimawalitsa dziko lonse; dziko lapansi limaona ndipo limanjenjemera.
Umbane wakhe ukhanyisa umhlaba; umhlaba ukubone lokho uthuthumele.
5 Mapiri amasungunuka ngati phula pamaso pa Yehova, pamaso pa Ambuye a dziko lonse lapansi.
Izintaba zincibilika njengengcino phambi kukaThixo, phambi kweNkosi yomhlaba wonke.
6 Mayiko akumwamba amalengeza za chilungamo chake, ndipo mitundu yonse ya anthu imaona ulemerero wake.
Amazulu amemezela ukulunga kwayo, labantu bonke bayayibona inkazimulo yayo.
7 Onse amene amalambira mafano osema amachititsidwa manyazi, iwo amene amanyadira mafano; mulambireni, inu milungu yonse!
Bonke abakhonza izifanekiso bathelwa ihlazo, labo abazikhukhumeza ngezithombe mkhonzeni, lonke lina bonkulunkulu!
8 Ziyoni akumva ndipo akukondwera, midzi ya Yuda ikusangalala chifukwa cha maweruzo anu Yehova.
IZiyoni iyezwa ithokoze lemizi yakoJuda iyajabula ngenxa yokwahlulela Kwakho, Oh Thixo.
9 Pakuti Inu Yehova ndi Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi; ndinu wokwezeka kupambana milungu yonse.
Ngoba wena, Oh Thixo ungoPhezukonke kuwo wonke umhlaba; uphakeme ngaphezulu kakhulu kwabonkulunkulu bonke.
10 Iwo amene amakonda Yehova adane ndi zoyipa pakuti Iye amayangʼanira miyoyo ya amene amamukhulupirira ndipo amawapulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa
Akuthi bonke abamthandayo, uThixo, bazonde okubi, ngoba uyazilinda impilo zabathembekileyo bakhe abakhulule esandleni sababi.
11 Kuwala kumafika pa anthu olungama, ndi chimwemwe kwa olungama mtima.
Ukukhanya kuyehliselwa kwabalungileyo lentokozo kwabaqotho enhliziyweni.
12 Kondwerani mwa Yehova Inu olungama ndipo tamandani dzina lake loyera.
Thokozani kuThixo lina elilungileyo, lidumise ibizo lakhe elingcwele.

< Masalimo 97 >