< Masalimo 97 >

1 Yehova akulamulira, dziko lapansi lisangalale; magombe akutali akondwere.
Huic David, quando terra ejus restituta est. [Dominus regnavit: exsultet terra; lætentur insulæ multæ.
2 Mitambo ndi mdima waukulu zamuzungulira; chilungamo ndi kuweruza molungama ndiwo maziko a mpando wake waufumu.
Nubes et caligo in circuitu ejus; justitia et judicium correctio sedis ejus.
3 Moto umapita patsogolo pake ndi kunyeketsa amaliwongo kumbali zonse.
Ignis ante ipsum præcedet, et inflammabit in circuitu inimicos ejus.
4 Zingʼaningʼani zake zimawalitsa dziko lonse; dziko lapansi limaona ndipo limanjenjemera.
Illuxerunt fulgura ejus orbi terræ; vidit, et commota est terra.
5 Mapiri amasungunuka ngati phula pamaso pa Yehova, pamaso pa Ambuye a dziko lonse lapansi.
Montes sicut cera fluxerunt a facie Domini; a facie Domini omnis terra.
6 Mayiko akumwamba amalengeza za chilungamo chake, ndipo mitundu yonse ya anthu imaona ulemerero wake.
Annuntiaverunt cæli justitiam ejus, et viderunt omnes populi gloriam ejus.
7 Onse amene amalambira mafano osema amachititsidwa manyazi, iwo amene amanyadira mafano; mulambireni, inu milungu yonse!
Confundantur omnes qui adorant sculptilia, et qui gloriantur in simulacris suis. Adorate eum omnes angeli ejus.
8 Ziyoni akumva ndipo akukondwera, midzi ya Yuda ikusangalala chifukwa cha maweruzo anu Yehova.
Audivit, et lætata est Sion, et exsultaverunt filiæ Judæ propter judicia tua, Domine.
9 Pakuti Inu Yehova ndi Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi; ndinu wokwezeka kupambana milungu yonse.
Quoniam tu Dominus altissimus super omnem terram; nimis exaltatus es super omnes deos.
10 Iwo amene amakonda Yehova adane ndi zoyipa pakuti Iye amayangʼanira miyoyo ya amene amamukhulupirira ndipo amawapulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa
Qui diligitis Dominum, odite malum: custodit Dominus animas sanctorum suorum; de manu peccatoris liberabit eos.
11 Kuwala kumafika pa anthu olungama, ndi chimwemwe kwa olungama mtima.
Lux orta est justo, et rectis corde lætitia.
12 Kondwerani mwa Yehova Inu olungama ndipo tamandani dzina lake loyera.
Lætamini, justi, in Domino, et confitemini memoriæ sanctificationis ejus.]

< Masalimo 97 >