< Masalimo 97 >

1 Yehova akulamulira, dziko lapansi lisangalale; magombe akutali akondwere.
Yahweh he reigns let it be glad the earth let them rejoice islands many.
2 Mitambo ndi mdima waukulu zamuzungulira; chilungamo ndi kuweruza molungama ndiwo maziko a mpando wake waufumu.
Cloud and thick darkness [are] around him [is] righteousness and justice [the] foundation of throne his.
3 Moto umapita patsogolo pake ndi kunyeketsa amaliwongo kumbali zonse.
Fire before him it goes and it may burn up all around opponents his.
4 Zingʼaningʼani zake zimawalitsa dziko lonse; dziko lapansi limaona ndipo limanjenjemera.
They light up lightning flashes his [the] world it sees and it trembled the earth.
5 Mapiri amasungunuka ngati phula pamaso pa Yehova, pamaso pa Ambuye a dziko lonse lapansi.
Mountains like wax they melt from to before Yahweh from to before [the] lord of all the earth.
6 Mayiko akumwamba amalengeza za chilungamo chake, ndipo mitundu yonse ya anthu imaona ulemerero wake.
They declare the heavens righteousness his and they see all the peoples glory his.
7 Onse amene amalambira mafano osema amachititsidwa manyazi, iwo amene amanyadira mafano; mulambireni, inu milungu yonse!
Let them be ashamed - all [those who] serve an image those [who] boast in worthless idols bow down to him O all gods.
8 Ziyoni akumva ndipo akukondwera, midzi ya Yuda ikusangalala chifukwa cha maweruzo anu Yehova.
It hears and it rejoiced - Zion and they were glad [the] daughters of Judah on account of judgments your O Yahweh.
9 Pakuti Inu Yehova ndi Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi; ndinu wokwezeka kupambana milungu yonse.
For you O Yahweh [are] most high over all the earth exceedingly you are exalted above all gods.
10 Iwo amene amakonda Yehova adane ndi zoyipa pakuti Iye amayangʼanira miyoyo ya amene amamukhulupirira ndipo amawapulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa
O [you who] love Yahweh hate evil [he is] protecting [the] lives of faithful [people] his from [the] hand of wicked [people] he delivers them.
11 Kuwala kumafika pa anthu olungama, ndi chimwemwe kwa olungama mtima.
Light [is] sown for the righteous and for [people] upright of heart joy.
12 Kondwerani mwa Yehova Inu olungama ndipo tamandani dzina lake loyera.
Rejoice O righteous [people] in Yahweh and give thanks to [the] remembrance of holiness his.

< Masalimo 97 >