< Masalimo 96 >
1 Imbirani Yehova nyimbo yatsopano; Imbirani Yehova dziko lonse lapansi.
Yeni bir ezgi söyleyin RAB'be! Ey bütün dünya, RAB'be ezgiler söyleyin!
2 Imbirani Yehova, tamandani dzina lake; lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
Ezgi söyleyin, RAB'bin adını övün, Her gün duyurun kurtarışını!
3 Lengezani ulemerero wake pakati pa mayiko, ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.
Görkemini uluslara, Harikalarını bütün halklara anlatın!
4 Pakuti wamkulu ndi Yehova ndipo ndi woyenera kwambiri kumutamanda; ayenera kuopedwa kupambana milungu yonse.
Çünkü RAB uludur, yalnız O övgüye değer, İlahlardan çok O'ndan korkulur.
5 Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano, koma Yehova analenga mayiko akumwamba.
Halkların bütün ilahları bir hiçtir, Oysa gökleri yaratan RAB'dir.
6 Ulemu ndi ufumu zili pamaso pake, mphamvu ndi ulemerero zili mʼmalo ake opatulika.
Yücelik, ululuk O'nun huzurundadır, Güç ve güzellik O'nun tapınağındadır.
7 Perekani kwa Yehova, inu mabanja a anthu a mitundu ina, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
Ey bütün halklar, RAB'bi övün, RAB'bin gücünü, yüceliğini övün,
8 Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake; bweretsani chopereka ndipo mulowe mʼmabwalo ake.
RAB'bin görkemini adına yaraşır biçimde övün, Sunular getirip avlularına girin!
9 Lambirani Yehova mu ulemerero wa chiyero chake; njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi.
Kutsal giysiler içinde RAB'be tapının! Titreyin O'nun önünde, ey bütün yeryüzündekiler!
10 Nenani pakati pa mitundu ya anthu, “Yehova akulamulira.” Dziko lonse lakhazikika molimba, silingasunthidwe; Iye adzaweruza mitundu ya anthu molungama.
Uluslara, “RAB egemenlik sürüyor” deyin. Dünya sağlam kurulmuş, sarsılmaz. O halkları adaletle yargılar.
11 Mayiko akumwamba asangalale, dziko lapansi likondwere; nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;
Sevinsin gökler, coşsun yeryüzü! Gürlesin deniz içindekilerle birlikte!
12 minda ikondwere pamodzi ndi chilichonse chili mʼmenemo. Pamenepo mitengo yonse ya mʼnkhalango idzayimba ndi chimwemwe;
Bayram etsin kırlar ve üzerindekiler! O zaman RAB'bin önünde bütün orman ağaçları Sevinçle haykıracak. Çünkü O geliyor! Yeryüzünü yargılamaya geliyor. Dünyayı adaletle, Halkları kendi gerçeğiyle yönetecek.
13 idzayimba pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi; adzaweruza dziko lonse mwachilungamo ndi mitundu ya anthu onse mʼchoonadi.