< Masalimo 96 >

1 Imbirani Yehova nyimbo yatsopano; Imbirani Yehova dziko lonse lapansi.
Cantád a Jehová canción nueva: cantád a Jehová toda la tierra.
2 Imbirani Yehova, tamandani dzina lake; lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
Cantád a Jehová, bendecíd su nombre: anunciád de día en día su salud.
3 Lengezani ulemerero wake pakati pa mayiko, ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.
Contád en las naciones su gloria: en todos los pueblos sus maravillas.
4 Pakuti wamkulu ndi Yehova ndipo ndi woyenera kwambiri kumutamanda; ayenera kuopedwa kupambana milungu yonse.
Porque grande es Jehová, y muy alabado: terrible sobre todos los dioses.
5 Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano, koma Yehova analenga mayiko akumwamba.
Porque todos los dioses de los pueblos son ídolos: mas Jehová hizo los cielos.
6 Ulemu ndi ufumu zili pamaso pake, mphamvu ndi ulemerero zili mʼmalo ake opatulika.
Alabanza y gloria está delante de él: fortaleza y gloria está en su santuario.
7 Perekani kwa Yehova, inu mabanja a anthu a mitundu ina, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
Dad a Jehová, o! familias de los pueblos, dad a Jehová la gloria y la fortaleza.
8 Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake; bweretsani chopereka ndipo mulowe mʼmabwalo ake.
Dad a Jehová la honra de su nombre: tomád presentes, y veníd a sus patios.
9 Lambirani Yehova mu ulemerero wa chiyero chake; njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi.
Encorváos a Jehová en la hermosura de su santuario: teméd delante de él toda la tierra.
10 Nenani pakati pa mitundu ya anthu, “Yehova akulamulira.” Dziko lonse lakhazikika molimba, silingasunthidwe; Iye adzaweruza mitundu ya anthu molungama.
Decíd en las naciones: Jehová reinó, también compuso el mundo, no se meneará: juzgará a los pueblos en justicia.
11 Mayiko akumwamba asangalale, dziko lapansi likondwere; nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;
Alégrense los cielos, y regocíjese la tierra: brame la mar y su plenitud.
12 minda ikondwere pamodzi ndi chilichonse chili mʼmenemo. Pamenepo mitengo yonse ya mʼnkhalango idzayimba ndi chimwemwe;
Regocíjese el campo y todo lo que en él está: entonces exultarán todos los árboles de la breña,
13 idzayimba pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi; adzaweruza dziko lonse mwachilungamo ndi mitundu ya anthu onse mʼchoonadi.
Delante de Jehová que vino: porque vino a juzgar la tierra. Juzgará al mundo con justicia, y a los pueblos con su verdad.

< Masalimo 96 >