< Masalimo 96 >

1 Imbirani Yehova nyimbo yatsopano; Imbirani Yehova dziko lonse lapansi.
Pjevajte Gospodu pjesmu novu, pjevaj Gospodu, sva zemljo!
2 Imbirani Yehova, tamandani dzina lake; lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
Pjevajte Gospodu, blagosiljajte ime njegovo, javljajte od dana na dan spasenje njegovo.
3 Lengezani ulemerero wake pakati pa mayiko, ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.
Kazujte po narodima slavu njegovu, po svijem plemenima èudesa njegova.
4 Pakuti wamkulu ndi Yehova ndipo ndi woyenera kwambiri kumutamanda; ayenera kuopedwa kupambana milungu yonse.
Jer je velik Gospod i valja ga hvaliti: strašniji je od svijeh bogova.
5 Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano, koma Yehova analenga mayiko akumwamba.
Jer su svi bogovi u naroda ništa: a Gospod je nebesa stvorio.
6 Ulemu ndi ufumu zili pamaso pake, mphamvu ndi ulemerero zili mʼmalo ake opatulika.
Slava je i velièanstvo pred licem njegovijem, (sila) i krasota u svetinji njegovoj.
7 Perekani kwa Yehova, inu mabanja a anthu a mitundu ina, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
Dajte Gospodu, plemena narodna, dajte Gospodu slavu i èast.
8 Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake; bweretsani chopereka ndipo mulowe mʼmabwalo ake.
Dajte Gospodu slavu prema imenu njegovu. Nosite dare i idite u dvore njegove.
9 Lambirani Yehova mu ulemerero wa chiyero chake; njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi.
Poklonite se Gospodu u svetoj krasoti. Strepi pred njim, sva zemljo!
10 Nenani pakati pa mitundu ya anthu, “Yehova akulamulira.” Dziko lonse lakhazikika molimba, silingasunthidwe; Iye adzaweruza mitundu ya anthu molungama.
Recite narodima: Gospod caruje; zato je vasiljena tvrda i neæe se pomjestiti; on æe suditi narodima pravo.
11 Mayiko akumwamba asangalale, dziko lapansi likondwere; nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;
Nek se vesele nebesa, i zemlja se raduje; nek pljeska more i što je u njemu;
12 minda ikondwere pamodzi ndi chilichonse chili mʼmenemo. Pamenepo mitengo yonse ya mʼnkhalango idzayimba ndi chimwemwe;
Neka skaèe polje i sve što je na njemu; tada nek se raduju sva drveta šumska
13 idzayimba pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi; adzaweruza dziko lonse mwachilungamo ndi mitundu ya anthu onse mʼchoonadi.
Pred licem Gospodnjim; jer ide, jer ide da sudi zemlji. Sudiæe vasiljenoj po pravdi, i narodima po istini svojoj.

< Masalimo 96 >