< Masalimo 96 >
1 Imbirani Yehova nyimbo yatsopano; Imbirani Yehova dziko lonse lapansi.
Cante para Yahweh uma nova canção! Cantem para Yahweh, toda a terra.
2 Imbirani Yehova, tamandani dzina lake; lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
Cante para Yahweh! Bendito seja seu nome! Proclamar sua salvação de dia para dia!
3 Lengezani ulemerero wake pakati pa mayiko, ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.
Declare sua glória entre as nações, suas obras maravilhosas entre todos os povos.
4 Pakuti wamkulu ndi Yehova ndipo ndi woyenera kwambiri kumutamanda; ayenera kuopedwa kupambana milungu yonse.
Para Yahweh é ótimo e muito louvável! Ele é para ser temido acima de todos os deuses.
5 Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano, koma Yehova analenga mayiko akumwamba.
Pois todos os deuses dos povos são ídolos, mas Yahweh fez os céus.
6 Ulemu ndi ufumu zili pamaso pake, mphamvu ndi ulemerero zili mʼmalo ake opatulika.
A honra e a majestade estão diante dele. A força e a beleza estão em seu santuário.
7 Perekani kwa Yehova, inu mabanja a anthu a mitundu ina, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
Atribuam a Yahweh, suas famílias de nações, atribuem a Yahweh glória e força.
8 Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake; bweretsani chopereka ndipo mulowe mʼmabwalo ake.
Atribua a Yahweh a glória devido a seu nome. Traga uma oferta, e venha a sua corte.
9 Lambirani Yehova mu ulemerero wa chiyero chake; njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi.
Adorar a Yahweh em santa disposição. Treme diante dele, toda a terra.
10 Nenani pakati pa mitundu ya anthu, “Yehova akulamulira.” Dziko lonse lakhazikika molimba, silingasunthidwe; Iye adzaweruza mitundu ya anthu molungama.
Diga entre as nações: “Yahweh reina”. O mundo também está estabelecido. Não pode ser movido. Ele julgará os povos com equidade.
11 Mayiko akumwamba asangalale, dziko lapansi likondwere; nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;
Que os céus se alegrem, e que a terra se regozije. Deixem o mar bramir, e sua plenitude!
12 minda ikondwere pamodzi ndi chilichonse chili mʼmenemo. Pamenepo mitengo yonse ya mʼnkhalango idzayimba ndi chimwemwe;
Let o campo e tudo o que há nele exultam! Então todas as árvores do bosque cantarão de alegria
13 idzayimba pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi; adzaweruza dziko lonse mwachilungamo ndi mitundu ya anthu onse mʼchoonadi.
antes de Yahweh; pois ele vem, pois ele vem para julgar a terra. Ele julgará o mundo com retidão, os povos com sua verdade.