< Masalimo 96 >
1 Imbirani Yehova nyimbo yatsopano; Imbirani Yehova dziko lonse lapansi.
Chantez en l'honneur de l'Éternel un cantique nouveau! Habitants de toute la terre, chantez en son honneur!
2 Imbirani Yehova, tamandani dzina lake; lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
Chantez en l'honneur de l'Éternel; bénissez son nom; Annoncez de jour en jour son oeuvre de salut!
3 Lengezani ulemerero wake pakati pa mayiko, ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.
Racontez sa gloire parmi les nations, Et ses merveilles parmi tous les peuples.
4 Pakuti wamkulu ndi Yehova ndipo ndi woyenera kwambiri kumutamanda; ayenera kuopedwa kupambana milungu yonse.
Car l'Éternel est grand et infiniment digne de louanges; Il est redoutable par-dessus tous les dieux.
5 Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano, koma Yehova analenga mayiko akumwamba.
Oui, tous les dieux des peuples sont des idoles; Mais l'Éternel a créé les cieux.
6 Ulemu ndi ufumu zili pamaso pake, mphamvu ndi ulemerero zili mʼmalo ake opatulika.
La splendeur et la majesté l'environnent; La force et la magnificence remplissent son sanctuaire.
7 Perekani kwa Yehova, inu mabanja a anthu a mitundu ina, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
Rendez à l'Éternel, familles des peuples. Rendez à l'Éternel la gloire et l'honneur!
8 Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake; bweretsani chopereka ndipo mulowe mʼmabwalo ake.
Rendez à l'Éternel la gloire due à son nom; Apportez des offrandes, et entrez dans ses parvis.
9 Lambirani Yehova mu ulemerero wa chiyero chake; njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi.
Prosternez-vous devant l'Éternel, Revêtus d'ornements sacrés. Tremblez devant lui, vous tous, habitants de la terre!
10 Nenani pakati pa mitundu ya anthu, “Yehova akulamulira.” Dziko lonse lakhazikika molimba, silingasunthidwe; Iye adzaweruza mitundu ya anthu molungama.
Dites parmi les nations: «L'Éternel est Roi; Aussi le monde est-il ferme, et il ne chancellera point. L'Éternel jugera les peuples avec équité.»
11 Mayiko akumwamba asangalale, dziko lapansi likondwere; nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;
Que les cieux se réjouissent, et que la terre tressaille de joie! Que la mer retentisse, avec tout ce qu'elle contient!
12 minda ikondwere pamodzi ndi chilichonse chili mʼmenemo. Pamenepo mitengo yonse ya mʼnkhalango idzayimba ndi chimwemwe;
Que les campagnes frémissent d'allégresse Avec tout ce qu'elles renferment; Que tous les arbres des forêts tressaillent de joie,
13 idzayimba pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi; adzaweruza dziko lonse mwachilungamo ndi mitundu ya anthu onse mʼchoonadi.
En présence de l'Éternel! Car il vient, il vient pour juger la terre! Il jugera le monde avec justice; Il jugera les nations, parce qu'il est fidèle à ses promesses.