< Masalimo 96 >

1 Imbirani Yehova nyimbo yatsopano; Imbirani Yehova dziko lonse lapansi.
Pakai kom ah lathah sauvin! Leiset pumpin Pakai vahchoila sauvin!
2 Imbirani Yehova, tamandani dzina lake; lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
Pakai vahchoila sauvin amin thangvah un. Ami huhhingna kipa umtah chu niseh’in samphongin.
3 Lengezani ulemerero wake pakati pa mayiko, ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.
Chitin namtin holah a athilbol kidangtah hohi samphong’in, Aman thil loupi tahtah abol hohi mijouse seipeh’un.
4 Pakuti wamkulu ndi Yehova ndipo ndi woyenera kwambiri kumutamanda; ayenera kuopedwa kupambana milungu yonse.
Pakai hi aloupi e! Amahi vahchoi dinga lompen ahi! Amahi pathen jouse sanga kichat umpentah ahi.
5 Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano, koma Yehova analenga mayiko akumwamba.
Chidang namdangho pathen hohi semthu pathen ngen ahiuve hinla Pakai hin vanho asem ahi!
6 Ulemu ndi ufumu zili pamaso pake, mphamvu ndi ulemerero zili mʼmalo ake opatulika.
Gin na le jana-in aumkimvel ahi, thahatna le melhoina hin muntheng alosoh ahi.
7 Perekani kwa Yehova, inu mabanja a anthu a mitundu ina, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
O chitin namtin vannoi mite ho, Pakai hethem un Pakai ahat nale aloupina hohi hethem un.
8 Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake; bweretsani chopereka ndipo mulowe mʼmabwalo ake.
Pakai chu achan dinga lomtah loupi nale jana chan sah’un! Nathilpeh ding kichoijin lang a-angsunga lut in.
9 Lambirani Yehova mu ulemerero wa chiyero chake; njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi.
Pakai chu athenna loupina vah chutoh kitohin chibai boh’un. Vannoi leiset pumpi hi a-angsungah kithing jenghen.
10 Nenani pakati pa mitundu ya anthu, “Yehova akulamulira.” Dziko lonse lakhazikika molimba, silingasunthidwe; Iye adzaweruza mitundu ya anthu molungama.
Chitin namtin hi seipeh un, “Pakai in vai ahom e!” Vannoi hi adingdetna ahitan holingbut ahitapon ahi.
11 Mayiko akumwamba asangalale, dziko lapansi likondwere; nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;
Vanho kipah hen chuleh vannoi leiset kipah-u hen! Twikhanglen leh asunga umjousen thangvah’un.
12 minda ikondwere pamodzi ndi chilichonse chili mʼmenemo. Pamenepo mitengo yonse ya mʼnkhalango idzayimba ndi chimwemwe;
Loujao holeh asunga kehho jouse jong kipahtah in hung gadoh sohkei uhen, gammang sunga thingphungho jousen jong
13 idzayimba pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi; adzaweruza dziko lonse mwachilungamo ndi mitundu ya anthu onse mʼchoonadi.
Pakai angsungah thangvah la sauhen, ajeh chu Ama ahungtai! Leiset chungthu tan dingin ahunge. Aman vannoi mite le chitin namtinhi kitahna-a achungthu atanding ahi.

< Masalimo 96 >