< Masalimo 95 >

1 Bwerani, tiyeni timuyimbire Yehova mwachimwemwe, tiyeni tifuwule kwa Thanthwe la chipulumutso chathu
Kommer, låter oss glädjas Herranom, och fröjdas för vår salighets tröst.
2 Tiyeni tibwere pamaso pake ndi chiyamiko ndipo mupembedzeni Iyeyo ndi zida zoyimbira ndi nyimbo.
Låt oss med tack komma inför hans ansigte, och fröjdas för honom med Psalmer.
3 Pakuti Yehova ndi Mulungu wamkulu, mfumu yayikulu pamwamba pa milungu yonse.
Ty Herren är en stor Gud, och en stor Konung öfver alla gudar.
4 Mʼmanja mwake muli maziko ozama a dziko lapansi, ndipo msonga za mapiri ndi zake.
Ty i hans hand är hvad som jorden bär, och bergshöjderna äro också hans.
5 Nyanja ndi yake, pakuti anayilenga ndi Iye, ndipo manja ake anawumba mtunda wowuma.
Ty hans är hafvet, och hans händer hafva det torra beredt.
6 Bwerani, tiyeni tiwerame pomulambira, tiyeni tigwade pamaso pa Yehova Mlengi wathu;
Kommer, låter oss tillbedja, och knäböja, och nederfalla för Herranom, den oss gjort hafver.
7 pakuti Iye ndiye Mulungu wathu ndipo ife ndife anthu a pabusa pake, ndi nkhosa za mʼdzanja lake. Lero ngati inu mumva mawu ake,
Ty han är vår Gud, och vi hans fosterfolk, och hans händers får.
8 musawumitse mitima yanu monga momwe munachitira pa Meriba, monga munachitira tsiku lija pa Masa mʼchipululu.
I dag om I hans röst hören, så förstocker icke edor hjerta, såsom i Meriba skedde, såsom i Massa i öknene;
9 Kumene makolo anu anandiyesa ndi kundiputa, ngakhale anaona zimene Ine ndinazichita.
Der edre fäder försökte mig, förnummo och sågo min verk;
10 Kwa zaka makumi anayi ndinali wokwiya ndi mʼbado umenewo; ndipo ndinati, “Iwo ndi anthu amene mitima yawo imasochera ndipo sanadziwe njira zanga.”
Att jag i fyratio år mödo hade med detta folk, och sade: Det är sådant folk, att deras hjerta alltid vill den orätta vägen, och de mina vägar icke lära vilja;
11 Choncho ndili chikwiyire, ndinalumbira kuti, “Iwowa sadzalowa ku malo anga a mpumulo.”
Så att jag svor i mine vrede: De skola icke komma till mina rolighet.

< Masalimo 95 >