< Masalimo 95 >

1 Bwerani, tiyeni timuyimbire Yehova mwachimwemwe, tiyeni tifuwule kwa Thanthwe la chipulumutso chathu
Nāciet, dziedāsim Tam Kungam priecīgi, gavilēsim savas pestīšanas patvērumam.
2 Tiyeni tibwere pamaso pake ndi chiyamiko ndipo mupembedzeni Iyeyo ndi zida zoyimbira ndi nyimbo.
Ejam priekš Viņa vaiga ar pateikšanu, gavilēsim Viņam ar dziesmām.
3 Pakuti Yehova ndi Mulungu wamkulu, mfumu yayikulu pamwamba pa milungu yonse.
Jo Tas Kungs ir tas lielais un stiprais Dievs un tas lielais ķēniņš pār visiem dieviem.
4 Mʼmanja mwake muli maziko ozama a dziko lapansi, ndipo msonga za mapiri ndi zake.
Viņa rokā ir zemes dziļumi, un kalnu augstumi Viņam pieder.
5 Nyanja ndi yake, pakuti anayilenga ndi Iye, ndipo manja ake anawumba mtunda wowuma.
Viņam pieder jūra, jo Viņš to radījis, un Viņa rokas sausumu ir cēlušas.
6 Bwerani, tiyeni tiwerame pomulambira, tiyeni tigwade pamaso pa Yehova Mlengi wathu;
Nāciet, pielūgsim, klanīsimies un metīsimies ceļos priekš Tā Kunga, sava radītāja.
7 pakuti Iye ndiye Mulungu wathu ndipo ife ndife anthu a pabusa pake, ndi nkhosa za mʼdzanja lake. Lero ngati inu mumva mawu ake,
Jo Viņš ir mūsu Dievs, un mēs esam Viņa ganības ļaudis un Viņa rokas avis.
8 musawumitse mitima yanu monga momwe munachitira pa Meriba, monga munachitira tsiku lija pa Masa mʼchipululu.
Šodien, kad jūs Viņa balsi dzirdiet, tad neapcietinājiet savas sirdis, tā kā Meribā, tā kā Masā tuksnesī,
9 Kumene makolo anu anandiyesa ndi kundiputa, ngakhale anaona zimene Ine ndinazichita.
Kur jūsu tēvi Mani kārdināja, Mani pārbaudīja, lai gan Manus darbus redzēja.
10 Kwa zaka makumi anayi ndinali wokwiya ndi mʼbado umenewo; ndipo ndinati, “Iwo ndi anthu amene mitima yawo imasochera ndipo sanadziwe njira zanga.”
Man četrdesmit gadus raizes ir bijušas ar šo tautu, tā ka Es sacīju: tie ir ļaudis, kam sirds maldās un kas Manus ceļus nepazīst.
11 Choncho ndili chikwiyire, ndinalumbira kuti, “Iwowa sadzalowa ku malo anga a mpumulo.”
Tādēļ Es Savā dusmībā esmu zvērējis: tiešām, tiem nebūs nākt pie Manas dusas.

< Masalimo 95 >