< Masalimo 95 >

1 Bwerani, tiyeni timuyimbire Yehova mwachimwemwe, tiyeni tifuwule kwa Thanthwe la chipulumutso chathu
Venez, chantons à Yahvé. Crions à haute voix vers le rocher de notre salut!
2 Tiyeni tibwere pamaso pake ndi chiyamiko ndipo mupembedzeni Iyeyo ndi zida zoyimbira ndi nyimbo.
Approchons-nous de sa présence avec des actions de grâce. Louons-le en chansons!
3 Pakuti Yehova ndi Mulungu wamkulu, mfumu yayikulu pamwamba pa milungu yonse.
Car Yahvé est un grand Dieu, un grand Roi au-dessus de tous les dieux.
4 Mʼmanja mwake muli maziko ozama a dziko lapansi, ndipo msonga za mapiri ndi zake.
Les profondeurs de la terre sont dans sa main. Les hauteurs des montagnes sont aussi les siennes.
5 Nyanja ndi yake, pakuti anayilenga ndi Iye, ndipo manja ake anawumba mtunda wowuma.
La mer est à lui, il l'a faite. Ses mains ont formé la terre ferme.
6 Bwerani, tiyeni tiwerame pomulambira, tiyeni tigwade pamaso pa Yehova Mlengi wathu;
Oh, venez, adorons et prosternons-nous. Agenouillons-nous devant Yahvé, notre créateur,
7 pakuti Iye ndiye Mulungu wathu ndipo ife ndife anthu a pabusa pake, ndi nkhosa za mʼdzanja lake. Lero ngati inu mumva mawu ake,
car il est notre Dieu. Nous sommes le peuple de son pâturage, et les moutons qu'il garde. Aujourd'hui, oh, que vous entendiez sa voix!
8 musawumitse mitima yanu monga momwe munachitira pa Meriba, monga munachitira tsiku lija pa Masa mʼchipululu.
N'endurcissez pas votre cœur, comme à Meriba, comme le jour de Massah dans le désert,
9 Kumene makolo anu anandiyesa ndi kundiputa, ngakhale anaona zimene Ine ndinazichita.
quand vos pères me tentaient, m'a testé, et a vu mon travail.
10 Kwa zaka makumi anayi ndinali wokwiya ndi mʼbado umenewo; ndipo ndinati, “Iwo ndi anthu amene mitima yawo imasochera ndipo sanadziwe njira zanga.”
Pendant quarante longues années, j'ai été affligé par cette génération, et a dit: « C'est un peuple qui se trompe dans son cœur. Ils n'ont pas connu mes voies. »
11 Choncho ndili chikwiyire, ndinalumbira kuti, “Iwowa sadzalowa ku malo anga a mpumulo.”
C'est pourquoi j'ai juré dans ma colère, « Ils n'entreront pas dans mon repos. »

< Masalimo 95 >