< Masalimo 95 >

1 Bwerani, tiyeni timuyimbire Yehova mwachimwemwe, tiyeni tifuwule kwa Thanthwe la chipulumutso chathu
O come, let us sing unto the Lord: let us shout joyfully to the rock of our salvation.
2 Tiyeni tibwere pamaso pake ndi chiyamiko ndipo mupembedzeni Iyeyo ndi zida zoyimbira ndi nyimbo.
Let us come before his presence with thanksgiving, and shout joyfully unto him with psalms.
3 Pakuti Yehova ndi Mulungu wamkulu, mfumu yayikulu pamwamba pa milungu yonse.
For a great God is the Lord, and a great King above all Gods;
4 Mʼmanja mwake muli maziko ozama a dziko lapansi, ndipo msonga za mapiri ndi zake.
In whose hand are the deep places of the earth; and whose are the heights of mountains;
5 Nyanja ndi yake, pakuti anayilenga ndi Iye, ndipo manja ake anawumba mtunda wowuma.
Whose is the sea, and who hath made it; and whose hands have formed the dry land.
6 Bwerani, tiyeni tiwerame pomulambira, tiyeni tigwade pamaso pa Yehova Mlengi wathu;
Oh come, let us prostrate ourselves and bow down: let us kneel before the Lord our Maker.
7 pakuti Iye ndiye Mulungu wathu ndipo ife ndife anthu a pabusa pake, ndi nkhosa za mʼdzanja lake. Lero ngati inu mumva mawu ake,
For he is our God; and we are the people of his pasture, and the flock of his hand: yea, this day, if ye will hearken to his voice,
8 musawumitse mitima yanu monga momwe munachitira pa Meriba, monga munachitira tsiku lija pa Masa mʼchipululu.
Harden not your heart, as at Meribah, as on the day of the temptation in the wilderness:
9 Kumene makolo anu anandiyesa ndi kundiputa, ngakhale anaona zimene Ine ndinazichita.
When your fathers tempted me, proved me, although they had seen my doing.
10 Kwa zaka makumi anayi ndinali wokwiya ndi mʼbado umenewo; ndipo ndinati, “Iwo ndi anthu amene mitima yawo imasochera ndipo sanadziwe njira zanga.”
Forty years long did I feel loathing on that generation, and I said, It is a people of an erring heart; and they truly acknowledged not my ways:
11 Choncho ndili chikwiyire, ndinalumbira kuti, “Iwowa sadzalowa ku malo anga a mpumulo.”
So that I swore in my wrath, that they should not enter into my rest.

< Masalimo 95 >