< Masalimo 94 >
1 Inu Yehova, ndinu Mulungu wobwezera chilango, Inu Mulungu amene mumabwezera chilango, wonetsani kuwala kwanu.
О Боже помсти, Господи, Боже помсти, з’яви Себе!
2 Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi; bwezerani kwa odzikuza zowayenera.
Піднімися, Судде землі, віддай гордим по заслугам!
3 Kodi mpaka liti anthu oyipa Inu Yehova, mpaka liti anthu oyipa adzalumpha ndi chimwemwe?
Аж доки нечестиві, Господи, доки нечестиві торжествувати будуть?
4 Amakhuthula mawu onyada; onse ochita zoyipa ndi odzaza ndi kudzikuza.
Вивергають, промовляють вони пиху, нахваляються всі, хто чинить гріх.
5 Amaphwanya anthu anu, Inu Yehova; amapondereza cholowa chanu.
Народ Твій, Господи, вони вражають ударами й пригнічують Твій спадок.
6 Amaphanso amayi a masiye ndi alendo okhala nawo mʼdziko; amapha ana amasiye.
Вдову й приходька вбивають, сироту гублять
7 Iwo amati, “Yehova sakuona; Mulungu wa Yakobo salabadirako.”
кажучи: «Не бачить Господь, і не вникає [в це] Бог Якова».
8 Samalani, inu anthu opanda nzeru pakati pa anthu; zitsiru inu, kodi mudzakhala liti anzeru?
Схаменіться, невігласи серед народу! Коли ви станете розумнішими, безумці?
9 Kodi Iye amene anapanga khutu sangathe kumva? Kodi Iye amene anapanga diso sangathe kuona?
Той, Хто насадив вухо, хіба не почує? Чи Той, Хто око створив, не побачить?
10 Kodi Iye amene amalangiza mitundu ya anthu sangathenso kulanga? Kodi Iye amene amaphunzitsa munthu angasowe nzeru?
Той, Хто народи карає, хіба не докорить? Той, Хто сам людині дає знання?
11 Yehova amadziwa maganizo a munthu; Iye amadziwa kuti maganizowo ndi achabechabe.
Господь знає думки людини, що вони – марнота.
12 Wodala munthu amene Inu Yehova mumamulangiza, munthu amene mumamuphunzitsa kuchokera mulamulo lanu;
Блаженний муж, якого Ти наставляєш, Господи, і Законом Твоїм навчаєш його,
13 mumamupumitsa pa nthawi ya mavuto, mpaka woyipa atakumbiridwa dzenje.
щоб заспокоїти його у дні лиха, поки буде викопана яма нечестивому!
14 Pakuti Yehova sadzawakana anthu ake; Iye sadzasiya cholowa chake.
Адже не покине Господь народу Свого й спадку Свого не полишить.
15 Chiweruzo chidzakhazikikanso pa chilungamo, ndipo onse olungama mtima adzachitsata.
Суд знову стане справедливим, і підуть услід за ним усі, праведні серцем.
16 Ndani adzadzuka chifukwa cha ine kulimbana ndi anthu oyipa? Ndani adzayimirira mʼmalo mwanga kulimbana ndi anthu ochita zoyipa?
Хто стане за мене проти злодіїв? Хто стоятиме за мене проти тих, що чинять гріх?
17 Yehova akanapanda kundithandiza, bwenzi nditakakhala msanga ku malo achete a imfa.
Якби Господь не був допомогою моєю, то оселилася б душа моя в [країні] мовчання.
18 Ndikanena kuti, “Phazi langa likuterereka,” chikondi chanu, Inu Yehova, chimandichirikiza.
Коли сказав я: «Хитається нога моя», милість Твоя, Господи, підтримала мене.
19 Pamene nkhawa inakula mʼkati mwanga, chitonthozo chanu chinabweretsa chimwemwe mʼmoyo mwanga.
Коли тривожні думки множаться в нутрі моєму, Твоя втіха збадьорює мою душу.
20 Kodi mpando waufumu woyipa ungathe kugwirizana nanu umene umabweretsa masautso chifukwa cha malamulo ake?
Хіба може мати щось спільне з Тобою престол загибелі, що діє всупереч постанові [Закону]?
21 Iwo amasonkhana pamodzi kulimbana ndi wolungama ndi kugamula kuti wosalakwa aphedwe.
Натовпом тиснуть вони на душу праведника, і кров невинну засуджують [на страту].
22 Koma Yehova wakhala linga langa, ndipo Mulungu ndiye thanthwe limene ndimathawirako.
Але Господь став моєю твердинею, і Бог мій – скеля мого притулку.
23 Iye adzawabwezera chifukwa cha machimo awo ndi kuwawononga chifukwa cha kuyipa kwawo; Yehova Mulungu wathu adzawawononga.
Він поверне проти них їхні власні гріхи і їхніми ж злодійствами знищить їх; знищить їх Господь, Бог наш.