< Masalimo 94 >

1 Inu Yehova, ndinu Mulungu wobwezera chilango, Inu Mulungu amene mumabwezera chilango, wonetsani kuwala kwanu.
Yahvé, tú, Dios a quien pertenece la venganza, tú, Dios, a quien pertenece la venganza, resplandece.
2 Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi; bwezerani kwa odzikuza zowayenera.
Levántate, juez de la tierra. Devuelve a los orgullosos lo que se merecen.
3 Kodi mpaka liti anthu oyipa Inu Yehova, mpaka liti anthu oyipa adzalumpha ndi chimwemwe?
Yahvé, hasta cuándo los malvados, ¿hasta cuándo triunfarán los malvados?
4 Amakhuthula mawu onyada; onse ochita zoyipa ndi odzaza ndi kudzikuza.
Derraman palabras arrogantes. Todos los malhechores se jactan.
5 Amaphwanya anthu anu, Inu Yehova; amapondereza cholowa chanu.
Rompen a tu pueblo en pedazos, Yahvé, y aflige tu herencia.
6 Amaphanso amayi a masiye ndi alendo okhala nawo mʼdziko; amapha ana amasiye.
Matan a la viuda y al extranjero, y asesinar a los huérfanos.
7 Iwo amati, “Yehova sakuona; Mulungu wa Yakobo salabadirako.”
Dicen: “Yah no verá, ni el Dios de Jacob considerará”.
8 Samalani, inu anthu opanda nzeru pakati pa anthu; zitsiru inu, kodi mudzakhala liti anzeru?
Considera, tú, insensato del pueblo; tontos, ¿cuándo seréis sabios?
9 Kodi Iye amene anapanga khutu sangathe kumva? Kodi Iye amene anapanga diso sangathe kuona?
El que implantó el oído, ¿no oirá? El que formó el ojo, ¿no verá?
10 Kodi Iye amene amalangiza mitundu ya anthu sangathenso kulanga? Kodi Iye amene amaphunzitsa munthu angasowe nzeru?
El que disciplina a las naciones, ¿no castigará? El que enseña al hombre sabe.
11 Yehova amadziwa maganizo a munthu; Iye amadziwa kuti maganizowo ndi achabechabe.
Yahvé conoce los pensamientos del hombre, que son inútiles.
12 Wodala munthu amene Inu Yehova mumamulangiza, munthu amene mumamuphunzitsa kuchokera mulamulo lanu;
Bendito es el hombre al que disciplinas, Yah, y enseñar con tu ley,
13 mumamupumitsa pa nthawi ya mavuto, mpaka woyipa atakumbiridwa dzenje.
para que le des descanso en los días de adversidad, hasta que la fosa sea cavada para los malvados.
14 Pakuti Yehova sadzawakana anthu ake; Iye sadzasiya cholowa chake.
Porque Yahvé no rechazará a su pueblo, ni abandonará su herencia.
15 Chiweruzo chidzakhazikikanso pa chilungamo, ndipo onse olungama mtima adzachitsata.
Porque el juicio volverá a la justicia. Todos los rectos de corazón la seguirán.
16 Ndani adzadzuka chifukwa cha ine kulimbana ndi anthu oyipa? Ndani adzayimirira mʼmalo mwanga kulimbana ndi anthu ochita zoyipa?
¿Quién se levantará por mí contra los malvados? ¿Quién me defenderá de los malhechores?
17 Yehova akanapanda kundithandiza, bwenzi nditakakhala msanga ku malo achete a imfa.
A menos que Yahvé haya sido mi ayuda, mi alma habría vivido pronto en el silencio.
18 Ndikanena kuti, “Phazi langa likuterereka,” chikondi chanu, Inu Yehova, chimandichirikiza.
Cuando dije: “¡Me resbala el pie!” Tu amorosa bondad, Yahvé, me sostuvo.
19 Pamene nkhawa inakula mʼkati mwanga, chitonthozo chanu chinabweretsa chimwemwe mʼmoyo mwanga.
En la multitud de mis pensamientos dentro de mí, tus consuelos deleitan mi alma.
20 Kodi mpando waufumu woyipa ungathe kugwirizana nanu umene umabweretsa masautso chifukwa cha malamulo ake?
El trono de la maldad tendrá comunión con vosotros, que provoca el malestar por el estatuto?
21 Iwo amasonkhana pamodzi kulimbana ndi wolungama ndi kugamula kuti wosalakwa aphedwe.
Se reúnen contra el alma del justo, y condenar la sangre inocente.
22 Koma Yehova wakhala linga langa, ndipo Mulungu ndiye thanthwe limene ndimathawirako.
Pero Yahvé ha sido mi alta torre, mi Dios, la roca de mi refugio.
23 Iye adzawabwezera chifukwa cha machimo awo ndi kuwawononga chifukwa cha kuyipa kwawo; Yehova Mulungu wathu adzawawononga.
Ha hecho recaer sobre ellos su propia iniquidad, y los cortará en su propia maldad. Yahvé, nuestro Dios, los cortará.

< Masalimo 94 >