< Masalimo 94 >

1 Inu Yehova, ndinu Mulungu wobwezera chilango, Inu Mulungu amene mumabwezera chilango, wonetsani kuwala kwanu.
Доамне, Думнезеул рэзбунэрилор, Ту, Думнезеул рэзбунэрилор, аратэ-Те!
2 Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi; bwezerani kwa odzikuza zowayenera.
Скоалэ-Те, Жудекэторул пэмынтулуй, ши рэсплэтеште челор мындри дупэ фаптеле лор!
3 Kodi mpaka liti anthu oyipa Inu Yehova, mpaka liti anthu oyipa adzalumpha ndi chimwemwe?
Пынэ кынд вор бируи чей рэй, Доамне, пынэ кынд вор бируи чей рэй?
4 Amakhuthula mawu onyada; onse ochita zoyipa ndi odzaza ndi kudzikuza.
Ей цин кувынтэрь путерниче, ворбеск ку труфие ши тоць чей че фак рэул се фэлеск.
5 Amaphwanya anthu anu, Inu Yehova; amapondereza cholowa chanu.
Ей здробеск пе попорул Тэу, Доамне, ши асупреск моштениря Та.
6 Amaphanso amayi a masiye ndi alendo okhala nawo mʼdziko; amapha ana amasiye.
Ынжунгие пе вэдувэ ши пе стрэин, учид пе орфань
7 Iwo amati, “Yehova sakuona; Mulungu wa Yakobo salabadirako.”
ши зик: „Ну веде Домнул ши Думнезеул луй Иаков ну я аминте!”
8 Samalani, inu anthu opanda nzeru pakati pa anthu; zitsiru inu, kodi mudzakhala liti anzeru?
Тотушь ынвэцаци-вэ минте, оамень фэрэ минте! Кынд вэ вець ынцелепци, небунилор?
9 Kodi Iye amene anapanga khutu sangathe kumva? Kodi Iye amene anapanga diso sangathe kuona?
Чел че а сэдит урекя с-ар путя сэ н-аудэ? Чел че а ынтокмит окюл с-ар путя сэ ну вадэ?
10 Kodi Iye amene amalangiza mitundu ya anthu sangathenso kulanga? Kodi Iye amene amaphunzitsa munthu angasowe nzeru?
Чел че педепсеште нямуриле с-ар путя сэ ну педепсяскэ, Ел, каре а дат омулуй причепере?
11 Yehova amadziwa maganizo a munthu; Iye amadziwa kuti maganizowo ndi achabechabe.
Домнул куноаште гындуриле омулуй: штие кэ сунт дешарте.
12 Wodala munthu amene Inu Yehova mumamulangiza, munthu amene mumamuphunzitsa kuchokera mulamulo lanu;
Фериче де омул пе каре-л педепсешть Ту, Доамне, ши пе каре-л ынвець дин Леӂя Та,
13 mumamupumitsa pa nthawi ya mavuto, mpaka woyipa atakumbiridwa dzenje.
ка сэ-л лиништешть ын зилеле ненорочирий, пынэ се ва сэпа гроапа челуй рэу!
14 Pakuti Yehova sadzawakana anthu ake; Iye sadzasiya cholowa chake.
Кэч Домнул ну ласэ пе попорул Сэу ши ну-Шь пэрэсеште моштениря.
15 Chiweruzo chidzakhazikikanso pa chilungamo, ndipo onse olungama mtima adzachitsata.
Чи се ва фаче одатэ жудеката дупэ дрептате ши тоць чей ку инима куратэ о вор гэси бунэ.
16 Ndani adzadzuka chifukwa cha ine kulimbana ndi anthu oyipa? Ndani adzayimirira mʼmalo mwanga kulimbana ndi anthu ochita zoyipa?
Чине мэ ва ажута ымпотрива челор рэй? Чине мэ ва сприжини ымпотрива челор че фак рэул?
17 Yehova akanapanda kundithandiza, bwenzi nditakakhala msanga ku malo achete a imfa.
Де н-ар фи Домнул ажуторул меу, кыт де курынд ар фи суфлетул меу ын тэчеря морций!
18 Ndikanena kuti, “Phazi langa likuterereka,” chikondi chanu, Inu Yehova, chimandichirikiza.
Орь де кыте орь зик: „Ми се клатинэ пичорул”, бунэтатя Та, Доамне, мэ сприжинэ тотдяуна.
19 Pamene nkhawa inakula mʼkati mwanga, chitonthozo chanu chinabweretsa chimwemwe mʼmoyo mwanga.
Кынд гындурь негре се фрэмынтэ ку грэмада ынэунтрул меу, мынгыериле Тале ымь ынвиорязэ суфлетул.
20 Kodi mpando waufumu woyipa ungathe kugwirizana nanu umene umabweretsa masautso chifukwa cha malamulo ake?
Те вор пуне чей рэй сэ шезь пе скаунул лор де домние, ей, каре прегэтеск ненорочиря ла адэпостул леӂий?
21 Iwo amasonkhana pamodzi kulimbana ndi wolungama ndi kugamula kuti wosalakwa aphedwe.
Ей се стрынг ымпотрива веций челуй неприхэнит ши осындеск сынӂе невиноват.
22 Koma Yehova wakhala linga langa, ndipo Mulungu ndiye thanthwe limene ndimathawirako.
Дар Домнул есте турнул меу де скэпаре, Думнезеул меу есте стынка мя де адэпост.
23 Iye adzawabwezera chifukwa cha machimo awo ndi kuwawononga chifukwa cha kuyipa kwawo; Yehova Mulungu wathu adzawawononga.
Ел ва фаче сэ кадэ асупра лор нелеӂюиря, Ел ый ва нимичи прин рэутатя лор; Домнул Думнезеул ностру ый ва нимичи.

< Masalimo 94 >