< Masalimo 94 >

1 Inu Yehova, ndinu Mulungu wobwezera chilango, Inu Mulungu amene mumabwezera chilango, wonetsani kuwala kwanu.
Psalmus ipsi David, quarta sabbati. [Deus ultionum Dominus; Deus ultionum libere egit.
2 Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi; bwezerani kwa odzikuza zowayenera.
Exaltare, qui judicas terram; redde retributionem superbis.
3 Kodi mpaka liti anthu oyipa Inu Yehova, mpaka liti anthu oyipa adzalumpha ndi chimwemwe?
Usquequo peccatores, Domine, usquequo peccatores gloriabuntur;
4 Amakhuthula mawu onyada; onse ochita zoyipa ndi odzaza ndi kudzikuza.
effabuntur et loquentur iniquitatem; loquentur omnes qui operantur injustitiam?
5 Amaphwanya anthu anu, Inu Yehova; amapondereza cholowa chanu.
Populum tuum, Domine, humiliaverunt, et hæreditatem tuam vexaverunt.
6 Amaphanso amayi a masiye ndi alendo okhala nawo mʼdziko; amapha ana amasiye.
Viduam et advenam interfecerunt, et pupillos occiderunt.
7 Iwo amati, “Yehova sakuona; Mulungu wa Yakobo salabadirako.”
Et dixerunt: Non videbit Dominus, nec intelliget Deus Jacob.
8 Samalani, inu anthu opanda nzeru pakati pa anthu; zitsiru inu, kodi mudzakhala liti anzeru?
Intelligite, insipientes in populo; et stulti, aliquando sapite.
9 Kodi Iye amene anapanga khutu sangathe kumva? Kodi Iye amene anapanga diso sangathe kuona?
Qui plantavit aurem non audiet? aut qui finxit oculum non considerat?
10 Kodi Iye amene amalangiza mitundu ya anthu sangathenso kulanga? Kodi Iye amene amaphunzitsa munthu angasowe nzeru?
Qui corripit gentes non arguet, qui docet hominem scientiam?
11 Yehova amadziwa maganizo a munthu; Iye amadziwa kuti maganizowo ndi achabechabe.
Dominus scit cogitationes hominum, quoniam vanæ sunt.
12 Wodala munthu amene Inu Yehova mumamulangiza, munthu amene mumamuphunzitsa kuchokera mulamulo lanu;
Beatus homo quem tu erudieris, Domine, et de lege tua docueris eum:
13 mumamupumitsa pa nthawi ya mavuto, mpaka woyipa atakumbiridwa dzenje.
ut mitiges ei a diebus malis, donec fodiatur peccatori fovea.
14 Pakuti Yehova sadzawakana anthu ake; Iye sadzasiya cholowa chake.
Quia non repellet Dominus plebem suam, et hæreditatem suam non derelinquet,
15 Chiweruzo chidzakhazikikanso pa chilungamo, ndipo onse olungama mtima adzachitsata.
quoadusque justitia convertatur in judicium: et qui juxta illam, omnes qui recto sunt corde.
16 Ndani adzadzuka chifukwa cha ine kulimbana ndi anthu oyipa? Ndani adzayimirira mʼmalo mwanga kulimbana ndi anthu ochita zoyipa?
Quis consurget mihi adversus malignantes? aut quis stabit mecum adversus operantes iniquitatem?
17 Yehova akanapanda kundithandiza, bwenzi nditakakhala msanga ku malo achete a imfa.
Nisi quia Dominus adjuvit me, paulominus habitasset in inferno anima mea. (questioned)
18 Ndikanena kuti, “Phazi langa likuterereka,” chikondi chanu, Inu Yehova, chimandichirikiza.
Si dicebam: Motus est pes meus: misericordia tua, Domine, adjuvabat me.
19 Pamene nkhawa inakula mʼkati mwanga, chitonthozo chanu chinabweretsa chimwemwe mʼmoyo mwanga.
Secundum multitudinem dolorum meorum in corde meo, consolationes tuæ lætificaverunt animam meam.
20 Kodi mpando waufumu woyipa ungathe kugwirizana nanu umene umabweretsa masautso chifukwa cha malamulo ake?
Numquid adhæret tibi sedes iniquitatis, qui fingis laborem in præcepto?
21 Iwo amasonkhana pamodzi kulimbana ndi wolungama ndi kugamula kuti wosalakwa aphedwe.
Captabunt in animam justi, et sanguinem innocentem condemnabunt.
22 Koma Yehova wakhala linga langa, ndipo Mulungu ndiye thanthwe limene ndimathawirako.
Et factus est mihi Dominus in refugium, et Deus meus in adjutorium spei meæ.
23 Iye adzawabwezera chifukwa cha machimo awo ndi kuwawononga chifukwa cha kuyipa kwawo; Yehova Mulungu wathu adzawawononga.
Et reddet illis iniquitatem ipsorum, et in malitia eorum disperdet eos: disperdet illos Dominus Deus noster.]

< Masalimo 94 >