< Masalimo 94 >

1 Inu Yehova, ndinu Mulungu wobwezera chilango, Inu Mulungu amene mumabwezera chilango, wonetsani kuwala kwanu.
Le Seigneur est le Dieu des vengeances: le Dieu des vengeances a agi avec liberté.
2 Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi; bwezerani kwa odzikuza zowayenera.
Levez-vous, vous qui jugez la terre: rendez leur salaire aux superbes.
3 Kodi mpaka liti anthu oyipa Inu Yehova, mpaka liti anthu oyipa adzalumpha ndi chimwemwe?
Jusqu’à quand les pécheurs, ô Seigneur, jusqu’à quand les pécheurs se glorifieront-ils?
4 Amakhuthula mawu onyada; onse ochita zoyipa ndi odzaza ndi kudzikuza.
Jusqu’à quand se répandront-ils en discours et parleront-ils iniquité? jusqu’à quand parleront-ils, tous ceux qui commettent l’injustice?
5 Amaphwanya anthu anu, Inu Yehova; amapondereza cholowa chanu.
Ils ont, Seigneur, humilié votre peuple; et votre héritage, ils l’ont ravagé.
6 Amaphanso amayi a masiye ndi alendo okhala nawo mʼdziko; amapha ana amasiye.
Ils ont massacré la veuve et l’étranger, et ils ont tué l’orphelin.
7 Iwo amati, “Yehova sakuona; Mulungu wa Yakobo salabadirako.”
Et ils ont dit: Le Seigneur ne le verra pas, et le Dieu de Jacob ne le saura pas.
8 Samalani, inu anthu opanda nzeru pakati pa anthu; zitsiru inu, kodi mudzakhala liti anzeru?
Comprenez, insensés du peuple; et vous, fous, devenez enfin sages.
9 Kodi Iye amene anapanga khutu sangathe kumva? Kodi Iye amene anapanga diso sangathe kuona?
Celui qui a fait l’oreille n’entendra-t-il pas? Celui qui a formé l’œil ne voit-il pas?
10 Kodi Iye amene amalangiza mitundu ya anthu sangathenso kulanga? Kodi Iye amene amaphunzitsa munthu angasowe nzeru?
Celui qui reprend des nations ne convaincra-t-il pas, lui qui enseigne à l’homme la science?
11 Yehova amadziwa maganizo a munthu; Iye amadziwa kuti maganizowo ndi achabechabe.
Le Seigneur sait que les pensées des hommes sont vaines.
12 Wodala munthu amene Inu Yehova mumamulangiza, munthu amene mumamuphunzitsa kuchokera mulamulo lanu;
Bienheureux l’homme que vous aurez vous-même instruit, Seigneur, et à qui vous aurez enseigné votre loi,
13 mumamupumitsa pa nthawi ya mavuto, mpaka woyipa atakumbiridwa dzenje.
Afin que vous lui accordiez quelque douceur dans des jours mauvais, jusqu’à ce qu’au pécheur soit creusée une fosse.
14 Pakuti Yehova sadzawakana anthu ake; Iye sadzasiya cholowa chake.
Parce que le Seigneur ne rejettera pas son peuple; et son héritage, il ne l’abandonnera pas.
15 Chiweruzo chidzakhazikikanso pa chilungamo, ndipo onse olungama mtima adzachitsata.
Jusqu’à ce que la justice se convertisse en jugement, et qu’auprès d’elle soient tous ceux qui ont le cœur droit.
16 Ndani adzadzuka chifukwa cha ine kulimbana ndi anthu oyipa? Ndani adzayimirira mʼmalo mwanga kulimbana ndi anthu ochita zoyipa?
Qui se lèvera pour moi contre des méchants? ou qui se tiendra près de moi contre des ouvriers d’iniquité?
17 Yehova akanapanda kundithandiza, bwenzi nditakakhala msanga ku malo achete a imfa.
Si ce n’était que le Seigneur m’a secouru, peu s’en serait fallu que dans l’enfer n’eût habité mon âme. (questioned)
18 Ndikanena kuti, “Phazi langa likuterereka,” chikondi chanu, Inu Yehova, chimandichirikiza.
Si je disais: Mon pied a chancelé, votre miséricorde, Seigneur, me venait en aide.
19 Pamene nkhawa inakula mʼkati mwanga, chitonthozo chanu chinabweretsa chimwemwe mʼmoyo mwanga.
Selon la multitude de mes douleurs qui étaient dans mon cœur, vos consolations ont réjoui mon âme.
20 Kodi mpando waufumu woyipa ungathe kugwirizana nanu umene umabweretsa masautso chifukwa cha malamulo ake?
Est-ce qu’un tribunal d’iniquité s’allie avec vous, qui faites d’un précepte un travail pénible?
21 Iwo amasonkhana pamodzi kulimbana ndi wolungama ndi kugamula kuti wosalakwa aphedwe.
Ils tendront des pièges à l’âme d’un juste, et condamneront un sang innocent.
22 Koma Yehova wakhala linga langa, ndipo Mulungu ndiye thanthwe limene ndimathawirako.
Mais le Seigneur est devenu pour moi un refuge; et mon Dieu, l’aide de mon espérance.
23 Iye adzawabwezera chifukwa cha machimo awo ndi kuwawononga chifukwa cha kuyipa kwawo; Yehova Mulungu wathu adzawawononga.
Et il leur rendra leur iniquité, il les perdra entièrement par leur malice; il les perdra entièrement, le Seigneur notre Dieu.

< Masalimo 94 >