< Masalimo 94 >
1 Inu Yehova, ndinu Mulungu wobwezera chilango, Inu Mulungu amene mumabwezera chilango, wonetsani kuwala kwanu.
Dieu des vengeances, Yahweh, Dieu des vengeances, parais!
2 Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi; bwezerani kwa odzikuza zowayenera.
Lève-toi, juge de la terre, rends aux superbes selon leurs œuvres!
3 Kodi mpaka liti anthu oyipa Inu Yehova, mpaka liti anthu oyipa adzalumpha ndi chimwemwe?
Jusques à quand les méchants, Yahweh, jusques à quand les méchants triompheront-ils?
4 Amakhuthula mawu onyada; onse ochita zoyipa ndi odzaza ndi kudzikuza.
Ils se répandent en discours arrogants, ils se glorifient, tous ces artisans d’iniquité.
5 Amaphwanya anthu anu, Inu Yehova; amapondereza cholowa chanu.
Yahweh, ils écrasent ton peuple, ils oppriment ton héritage,
6 Amaphanso amayi a masiye ndi alendo okhala nawo mʼdziko; amapha ana amasiye.
ils égorgent la veuve et l’étranger, ils massacrent les orphelins.
7 Iwo amati, “Yehova sakuona; Mulungu wa Yakobo salabadirako.”
Et ils disent: « Yahweh ne regarde pas, le Dieu de Jacob ne fait pas attention. »
8 Samalani, inu anthu opanda nzeru pakati pa anthu; zitsiru inu, kodi mudzakhala liti anzeru?
Comprenez-donc, stupides enfants du peuple! Insensés, quand aurez-vous l’intelligence?
9 Kodi Iye amene anapanga khutu sangathe kumva? Kodi Iye amene anapanga diso sangathe kuona?
Celui qui a planté l’oreille n’entendrait-il pas? Celui qui a formé l’œil ne verrait-il pas?
10 Kodi Iye amene amalangiza mitundu ya anthu sangathenso kulanga? Kodi Iye amene amaphunzitsa munthu angasowe nzeru?
Celui qui châtie les nations ne punirait-il pas? Celui qui donne à l’homme l’intelligence ne reconnaîtrait-il pas?
11 Yehova amadziwa maganizo a munthu; Iye amadziwa kuti maganizowo ndi achabechabe.
Yahweh connaît les pensées des hommes, il sait qu’elles sont vaines.
12 Wodala munthu amene Inu Yehova mumamulangiza, munthu amene mumamuphunzitsa kuchokera mulamulo lanu;
Heureux l’homme que tu instruis, Yahweh, et à qui tu donnes l’enseignement de ta loi,
13 mumamupumitsa pa nthawi ya mavuto, mpaka woyipa atakumbiridwa dzenje.
pour l’apaiser aux jours du malheur, jusqu’à ce que la fosse soit creusée pour le méchant.
14 Pakuti Yehova sadzawakana anthu ake; Iye sadzasiya cholowa chake.
Car Yahweh ne rejettera pas son peuple, il n’abandonnera pas son héritage;
15 Chiweruzo chidzakhazikikanso pa chilungamo, ndipo onse olungama mtima adzachitsata.
mais le jugement redeviendra conforme à la justice, et tous les hommes au cœur droit y applaudiront.
16 Ndani adzadzuka chifukwa cha ine kulimbana ndi anthu oyipa? Ndani adzayimirira mʼmalo mwanga kulimbana ndi anthu ochita zoyipa?
Qui se lèvera pour moi contre les méchants? Qui me soutiendra contre ceux qui font le mal?
17 Yehova akanapanda kundithandiza, bwenzi nditakakhala msanga ku malo achete a imfa.
Si Yahweh n’était pas mon secours, mon âme habiterait bientôt le séjour du silence.
18 Ndikanena kuti, “Phazi langa likuterereka,” chikondi chanu, Inu Yehova, chimandichirikiza.
Quand je dis: « Mon pied chancelle, » ta bonté, Yahweh, me soutient.
19 Pamene nkhawa inakula mʼkati mwanga, chitonthozo chanu chinabweretsa chimwemwe mʼmoyo mwanga.
Quand les angoisses s’agitent en foule dans ma pensée, tes consolations réjouissent mon âme.
20 Kodi mpando waufumu woyipa ungathe kugwirizana nanu umene umabweretsa masautso chifukwa cha malamulo ake?
A-t-il rien de commun avec toi le tribunal de perdition, qui fait le mal dans les formes légales?
21 Iwo amasonkhana pamodzi kulimbana ndi wolungama ndi kugamula kuti wosalakwa aphedwe.
Ils s’empressent contre la vie du juste, et ils condamnent le sang innocent.
22 Koma Yehova wakhala linga langa, ndipo Mulungu ndiye thanthwe limene ndimathawirako.
Mais Yahweh est ma forteresse, mon Dieu est le rocher où je m’abrite.
23 Iye adzawabwezera chifukwa cha machimo awo ndi kuwawononga chifukwa cha kuyipa kwawo; Yehova Mulungu wathu adzawawononga.
Il fera retomber sur eux leur iniquité, il les exterminera par leur propre malice, il les exterminera, Yahweh, notre Dieu!