< Masalimo 94 >

1 Inu Yehova, ndinu Mulungu wobwezera chilango, Inu Mulungu amene mumabwezera chilango, wonetsani kuwala kwanu.
Herra Jumala, jonka kostot ovat, Jumala, jonka kostot ovat, selkiästi itses näytä.
2 Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi; bwezerani kwa odzikuza zowayenera.
Korota sinuas, maailman tuomari: maksa ylpeille, mitä he ansainneet ovat.
3 Kodi mpaka liti anthu oyipa Inu Yehova, mpaka liti anthu oyipa adzalumpha ndi chimwemwe?
Herra, kuinka kauvan pitää jumalattomain, kuinka kauvan pitää jumalattomain riemuitseman?
4 Amakhuthula mawu onyada; onse ochita zoyipa ndi odzaza ndi kudzikuza.
Tiuskuman ja puhuman niin ylpiästi, ja kaikki pahantekiät niin kerskaaman?
5 Amaphwanya anthu anu, Inu Yehova; amapondereza cholowa chanu.
Herra, he polkevat alas sinun kansas, ja sinun perimistäs he vaivaavat.
6 Amaphanso amayi a masiye ndi alendo okhala nawo mʼdziko; amapha ana amasiye.
Lesket ja muukalaiset he tappavat, ja orvot he kuolettavat,
7 Iwo amati, “Yehova sakuona; Mulungu wa Yakobo salabadirako.”
Ja sanovat: ei Herra sitä näe, ja Jakobin Jumala ei sitä tottele.
8 Samalani, inu anthu opanda nzeru pakati pa anthu; zitsiru inu, kodi mudzakhala liti anzeru?
Ymmärtäkäät siis, te hullut kansan seassa! ja, te tyhmät, koska te taitaviksi tulette?
9 Kodi Iye amene anapanga khutu sangathe kumva? Kodi Iye amene anapanga diso sangathe kuona?
Joka korvan on istuttanut, eikö hän kuule? eli joka silmän loi, eikö hän näe?
10 Kodi Iye amene amalangiza mitundu ya anthu sangathenso kulanga? Kodi Iye amene amaphunzitsa munthu angasowe nzeru?
Joka pakanoita kurittaa, eikö hän rankaise, joka ihmisille opettaa tiedon?
11 Yehova amadziwa maganizo a munthu; Iye amadziwa kuti maganizowo ndi achabechabe.
Mutta Herra tietää ihmisten ajatukset, että ne turhat ovat.
12 Wodala munthu amene Inu Yehova mumamulangiza, munthu amene mumamuphunzitsa kuchokera mulamulo lanu;
Autuas on se, jota sinä, Herra, kuritat, ja opetat sinun laistas,
13 mumamupumitsa pa nthawi ya mavuto, mpaka woyipa atakumbiridwa dzenje.
Että hänellä kärsivällisyys olis, koska vastoin käy, siihenasti kuin jumalattomalle hauta valmistetaan.
14 Pakuti Yehova sadzawakana anthu ake; Iye sadzasiya cholowa chake.
Sillä ei Herra heitä kansaansa pois, eli hylkää perimistänsä.
15 Chiweruzo chidzakhazikikanso pa chilungamo, ndipo onse olungama mtima adzachitsata.
Sillä oikeuden pitää sittekin oikeuden oleman, ja kaikki hurskaat sydämet sitä seuraavat.
16 Ndani adzadzuka chifukwa cha ine kulimbana ndi anthu oyipa? Ndani adzayimirira mʼmalo mwanga kulimbana ndi anthu ochita zoyipa?
Kuka seisoo minun kanssani pahoja vastaan? kuka astuu minun tyköni pahointekiöitä vastaan?
17 Yehova akanapanda kundithandiza, bwenzi nditakakhala msanga ku malo achete a imfa.
Ellei Herra minua auttaisi, niin minun sieluni makais lähes hiljaisuudessa.
18 Ndikanena kuti, “Phazi langa likuterereka,” chikondi chanu, Inu Yehova, chimandichirikiza.
Minä sanoin: minun jalkani on horjunut, vaan sinun armos, Herra, minun tukesi.
19 Pamene nkhawa inakula mʼkati mwanga, chitonthozo chanu chinabweretsa chimwemwe mʼmoyo mwanga.
Minulla oli paljo surua sydämessäni; mutta sinun lohdutukses ilahutti minun sieluni.
20 Kodi mpando waufumu woyipa ungathe kugwirizana nanu umene umabweretsa masautso chifukwa cha malamulo ake?
Etpäs mielisty koskaan tosin vahingolliseen istuimeen, joka lain häijysti opettaa.
21 Iwo amasonkhana pamodzi kulimbana ndi wolungama ndi kugamula kuti wosalakwa aphedwe.
He kokoovat joukkonsa vanhurskaan sielua vastaan, ja tuomitsevat viattoman veren kadotukseen,
22 Koma Yehova wakhala linga langa, ndipo Mulungu ndiye thanthwe limene ndimathawirako.
Mutta Herra on minun varjelukseni: minun Jumalani on minun uskallukseni turva,
23 Iye adzawabwezera chifukwa cha machimo awo ndi kuwawononga chifukwa cha kuyipa kwawo; Yehova Mulungu wathu adzawawononga.
Ja hän kostaa heidän vääryytensä, ja hukuttaa heitä heidän pahuutensa tähden: Herra, meidän Jumalamme, hukuttaa heitä.

< Masalimo 94 >