< Masalimo 94 >

1 Inu Yehova, ndinu Mulungu wobwezera chilango, Inu Mulungu amene mumabwezera chilango, wonetsani kuwala kwanu.
YHWH, you God to whom vengeance belongs, you God to whom vengeance belongs, shine forth.
2 Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi; bwezerani kwa odzikuza zowayenera.
Rise up, you judge of the earth. Pay back the proud what they deserve.
3 Kodi mpaka liti anthu oyipa Inu Yehova, mpaka liti anthu oyipa adzalumpha ndi chimwemwe?
YHWH, how long will the wicked, how long will the wicked triumph?
4 Amakhuthula mawu onyada; onse ochita zoyipa ndi odzaza ndi kudzikuza.
They pour out arrogant words. All the evildoers boast.
5 Amaphwanya anthu anu, Inu Yehova; amapondereza cholowa chanu.
They break your people in pieces, YHWH, and afflict your heritage.
6 Amaphanso amayi a masiye ndi alendo okhala nawo mʼdziko; amapha ana amasiye.
They kill the widow and the alien, and murder the fatherless.
7 Iwo amati, “Yehova sakuona; Mulungu wa Yakobo salabadirako.”
They say, "JAH will not see, neither will Jacob's God consider."
8 Samalani, inu anthu opanda nzeru pakati pa anthu; zitsiru inu, kodi mudzakhala liti anzeru?
Consider, you senseless among the people; you fools, when will you be wise?
9 Kodi Iye amene anapanga khutu sangathe kumva? Kodi Iye amene anapanga diso sangathe kuona?
He who implanted the ear, won't he hear? He who formed the eye, won't he see?
10 Kodi Iye amene amalangiza mitundu ya anthu sangathenso kulanga? Kodi Iye amene amaphunzitsa munthu angasowe nzeru?
He who disciplines the nations, won't he punish? He who teaches man knows.
11 Yehova amadziwa maganizo a munthu; Iye amadziwa kuti maganizowo ndi achabechabe.
YHWH knows the thoughts of man, that they are futile.
12 Wodala munthu amene Inu Yehova mumamulangiza, munthu amene mumamuphunzitsa kuchokera mulamulo lanu;
Blessed is the man whom you discipline, JAH, and teach out of your Law;
13 mumamupumitsa pa nthawi ya mavuto, mpaka woyipa atakumbiridwa dzenje.
that you may give him rest from the days of adversity, until the pit is dug for the wicked.
14 Pakuti Yehova sadzawakana anthu ake; Iye sadzasiya cholowa chake.
For YHWH won't reject his people, neither will he forsake his inheritance.
15 Chiweruzo chidzakhazikikanso pa chilungamo, ndipo onse olungama mtima adzachitsata.
For judgment will return to righteousness. All the upright in heart shall follow it.
16 Ndani adzadzuka chifukwa cha ine kulimbana ndi anthu oyipa? Ndani adzayimirira mʼmalo mwanga kulimbana ndi anthu ochita zoyipa?
Who will rise up for me against the wicked? Who will stand up for me against the evildoers?
17 Yehova akanapanda kundithandiza, bwenzi nditakakhala msanga ku malo achete a imfa.
Unless YHWH had been my help, my soul would have soon lived in silence.
18 Ndikanena kuti, “Phazi langa likuterereka,” chikondi chanu, Inu Yehova, chimandichirikiza.
When I said, "My foot is slipping." Your loving kindness, YHWH, held me up.
19 Pamene nkhawa inakula mʼkati mwanga, chitonthozo chanu chinabweretsa chimwemwe mʼmoyo mwanga.
In the multitude of my thoughts within me, your comforts delight my soul.
20 Kodi mpando waufumu woyipa ungathe kugwirizana nanu umene umabweretsa masautso chifukwa cha malamulo ake?
Shall the throne of wickedness have fellowship with you, which brings about mischief by statute?
21 Iwo amasonkhana pamodzi kulimbana ndi wolungama ndi kugamula kuti wosalakwa aphedwe.
They gather themselves together against the soul of the righteous, and condemn the innocent blood.
22 Koma Yehova wakhala linga langa, ndipo Mulungu ndiye thanthwe limene ndimathawirako.
But YHWH has been my high tower, my God, the rock of my refuge.
23 Iye adzawabwezera chifukwa cha machimo awo ndi kuwawononga chifukwa cha kuyipa kwawo; Yehova Mulungu wathu adzawawononga.
He has brought on them their own iniquity, and will cut them off in their own wickedness. YHWH, our God, will cut them off.

< Masalimo 94 >