< Masalimo 94 >

1 Inu Yehova, ndinu Mulungu wobwezera chilango, Inu Mulungu amene mumabwezera chilango, wonetsani kuwala kwanu.
God of vengeance—YHWH! God of vengeance, shine forth.
2 Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi; bwezerani kwa odzikuza zowayenera.
Be lifted up, judging the earth, Send back a repayment on the proud.
3 Kodi mpaka liti anthu oyipa Inu Yehova, mpaka liti anthu oyipa adzalumpha ndi chimwemwe?
Until when do the wicked, O YHWH—Until when do the wicked exult?
4 Amakhuthula mawu onyada; onse ochita zoyipa ndi odzaza ndi kudzikuza.
They utter—they speak arrogance, All working iniquity boast [about] themselves.
5 Amaphwanya anthu anu, Inu Yehova; amapondereza cholowa chanu.
Your people, O YHWH, they bruise, And they afflict Your inheritance.
6 Amaphanso amayi a masiye ndi alendo okhala nawo mʼdziko; amapha ana amasiye.
They slay widow and sojourner, And they murder fatherless ones.
7 Iwo amati, “Yehova sakuona; Mulungu wa Yakobo salabadirako.”
And they say, “YAH does not see, And the God of Jacob does not consider.”
8 Samalani, inu anthu opanda nzeru pakati pa anthu; zitsiru inu, kodi mudzakhala liti anzeru?
Consider, you brutish among the people, And you foolish, when do you act wisely?
9 Kodi Iye amene anapanga khutu sangathe kumva? Kodi Iye amene anapanga diso sangathe kuona?
He who plants the ear, does He not hear? He who forms the eye, does He not see?
10 Kodi Iye amene amalangiza mitundu ya anthu sangathenso kulanga? Kodi Iye amene amaphunzitsa munthu angasowe nzeru?
He who is instructing nations, does He not reprove? He who is teaching man knowledge [is] YHWH.
11 Yehova amadziwa maganizo a munthu; Iye amadziwa kuti maganizowo ndi achabechabe.
He knows the thoughts of man, that they [are] vanity.
12 Wodala munthu amene Inu Yehova mumamulangiza, munthu amene mumamuphunzitsa kuchokera mulamulo lanu;
O the blessedness of the man Whom You instruct, O YAH, And teach him out of Your law,
13 mumamupumitsa pa nthawi ya mavuto, mpaka woyipa atakumbiridwa dzenje.
To give rest to him from days of evil, While a pit is dug for the wicked.
14 Pakuti Yehova sadzawakana anthu ake; Iye sadzasiya cholowa chake.
For YHWH does not leave His people, And does not forsake His inheritance.
15 Chiweruzo chidzakhazikikanso pa chilungamo, ndipo onse olungama mtima adzachitsata.
For judgment turns back to righteousness, And after it all the upright of heart.
16 Ndani adzadzuka chifukwa cha ine kulimbana ndi anthu oyipa? Ndani adzayimirira mʼmalo mwanga kulimbana ndi anthu ochita zoyipa?
Who rises up for me with evildoers? Who stations himself for me with workers of iniquity?
17 Yehova akanapanda kundithandiza, bwenzi nditakakhala msanga ku malo achete a imfa.
Unless YHWH [were] a help to me, My soul had almost inhabited silence.
18 Ndikanena kuti, “Phazi langa likuterereka,” chikondi chanu, Inu Yehova, chimandichirikiza.
If I have said, “My foot has slipped,” Your kindness, O YHWH, supports me.
19 Pamene nkhawa inakula mʼkati mwanga, chitonthozo chanu chinabweretsa chimwemwe mʼmoyo mwanga.
In the abundance of my thoughts within me, Your comforts delight my soul.
20 Kodi mpando waufumu woyipa ungathe kugwirizana nanu umene umabweretsa masautso chifukwa cha malamulo ake?
Is a throne of mischief joined [with] You? A framer of perverseness by statute?
21 Iwo amasonkhana pamodzi kulimbana ndi wolungama ndi kugamula kuti wosalakwa aphedwe.
They decree against the soul of the righteous, And declare innocent blood wicked.
22 Koma Yehova wakhala linga langa, ndipo Mulungu ndiye thanthwe limene ndimathawirako.
And YHWH is for a high place to me, And my God [is] for a rock—my refuge,
23 Iye adzawabwezera chifukwa cha machimo awo ndi kuwawononga chifukwa cha kuyipa kwawo; Yehova Mulungu wathu adzawawononga.
And He turns back their iniquity on them, And in their wickedness cuts them off; Our God YHWH cuts them off!

< Masalimo 94 >