< Masalimo 94 >
1 Inu Yehova, ndinu Mulungu wobwezera chilango, Inu Mulungu amene mumabwezera chilango, wonetsani kuwala kwanu.
A Psalm of David himself. The Fourth Sabbath. The Lord is the God of retribution. The God of retribution acts in order to deliver.
2 Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi; bwezerani kwa odzikuza zowayenera.
Lift yourself up, for you judge the earth. Repay the arrogant with retribution.
3 Kodi mpaka liti anthu oyipa Inu Yehova, mpaka liti anthu oyipa adzalumpha ndi chimwemwe?
How long will sinners, O Lord, how long will sinners glory?
4 Amakhuthula mawu onyada; onse ochita zoyipa ndi odzaza ndi kudzikuza.
How long will they utter and speak iniquity? How long will all who work injustice speak out?
5 Amaphwanya anthu anu, Inu Yehova; amapondereza cholowa chanu.
They have humiliated your people, O Lord, and they have harassed your inheritance.
6 Amaphanso amayi a masiye ndi alendo okhala nawo mʼdziko; amapha ana amasiye.
They have executed the widow and the new arrival, and they have slaughtered the orphan.
7 Iwo amati, “Yehova sakuona; Mulungu wa Yakobo salabadirako.”
And they have said, “The Lord will not see, nor will the God of Jacob understand.”
8 Samalani, inu anthu opanda nzeru pakati pa anthu; zitsiru inu, kodi mudzakhala liti anzeru?
Understand, you senseless ones among the people. And be wise at last, you foolish ones.
9 Kodi Iye amene anapanga khutu sangathe kumva? Kodi Iye amene anapanga diso sangathe kuona?
He who formed the ear, will he not hear? And he who forged the eye, does he not look closely?
10 Kodi Iye amene amalangiza mitundu ya anthu sangathenso kulanga? Kodi Iye amene amaphunzitsa munthu angasowe nzeru?
He who chastises nations, he who teaches man knowledge, will he not rebuke?
11 Yehova amadziwa maganizo a munthu; Iye amadziwa kuti maganizowo ndi achabechabe.
The Lord knows the thoughts of men: that these are in vain.
12 Wodala munthu amene Inu Yehova mumamulangiza, munthu amene mumamuphunzitsa kuchokera mulamulo lanu;
Blessed is the man whom you will instruct, O Lord. And you will teach him from your law.
13 mumamupumitsa pa nthawi ya mavuto, mpaka woyipa atakumbiridwa dzenje.
So may you soothe him from the evil days, until a pit may be dug for sinners.
14 Pakuti Yehova sadzawakana anthu ake; Iye sadzasiya cholowa chake.
For the Lord will not drive away his people, and he will not abandon his inheritance,
15 Chiweruzo chidzakhazikikanso pa chilungamo, ndipo onse olungama mtima adzachitsata.
even until the time when justice is being converted into judgment, and when those who are close to justice are all those who are upright of heart.
16 Ndani adzadzuka chifukwa cha ine kulimbana ndi anthu oyipa? Ndani adzayimirira mʼmalo mwanga kulimbana ndi anthu ochita zoyipa?
Who will rise up with me against the malignant? Or who will stand with me against the workers of iniquity?
17 Yehova akanapanda kundithandiza, bwenzi nditakakhala msanga ku malo achete a imfa.
Except that the Lord assisted me, my soul almost would have dwelt in Hell. ()
18 Ndikanena kuti, “Phazi langa likuterereka,” chikondi chanu, Inu Yehova, chimandichirikiza.
If ever I said, “My foot is slipping,” then your mercy, O Lord, assisted me.
19 Pamene nkhawa inakula mʼkati mwanga, chitonthozo chanu chinabweretsa chimwemwe mʼmoyo mwanga.
According to the multitude of my sorrows in my heart, your consolations have given joy to my soul.
20 Kodi mpando waufumu woyipa ungathe kugwirizana nanu umene umabweretsa masautso chifukwa cha malamulo ake?
Does the seat of iniquity adhere to you, you who contrive hardship within a commandment?
21 Iwo amasonkhana pamodzi kulimbana ndi wolungama ndi kugamula kuti wosalakwa aphedwe.
They will hunt down the soul of the just, and they will condemn innocent blood.
22 Koma Yehova wakhala linga langa, ndipo Mulungu ndiye thanthwe limene ndimathawirako.
And the Lord has been made into a refuge for me, and my God into the assistance of my hope.
23 Iye adzawabwezera chifukwa cha machimo awo ndi kuwawononga chifukwa cha kuyipa kwawo; Yehova Mulungu wathu adzawawononga.
And he will repay them their iniquity, and he will destroy them in their malice. The Lord our God will utterly destroy them.