< Masalimo 94 >

1 Inu Yehova, ndinu Mulungu wobwezera chilango, Inu Mulungu amene mumabwezera chilango, wonetsani kuwala kwanu.
Bože osvetniče, Jahve, Bože osvetniče, pokaži se.
2 Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi; bwezerani kwa odzikuza zowayenera.
Ustani ti što sudiš zemlju, po zasluzi plati oholima!
3 Kodi mpaka liti anthu oyipa Inu Yehova, mpaka liti anthu oyipa adzalumpha ndi chimwemwe?
Dokle će bezbošci, Jahve, dokle će se bezbošci hvastati?
4 Amakhuthula mawu onyada; onse ochita zoyipa ndi odzaza ndi kudzikuza.
Dokle će brbljati, drsko govoriti, dokle će se bezakonici hvastati?
5 Amaphwanya anthu anu, Inu Yehova; amapondereza cholowa chanu.
Tlače narod tvoj, Jahve, i baštinu tvoju pritišću;
6 Amaphanso amayi a masiye ndi alendo okhala nawo mʼdziko; amapha ana amasiye.
kolju udovicu i pridošlicu, sirotama život oduzimlju
7 Iwo amati, “Yehova sakuona; Mulungu wa Yakobo salabadirako.”
i govore: “Jahve ne vidi! Ne opaža Bog Jakovljev!”
8 Samalani, inu anthu opanda nzeru pakati pa anthu; zitsiru inu, kodi mudzakhala liti anzeru?
Shvatite, lude u narodu: bezumni, kad ćete se urazumiti?
9 Kodi Iye amene anapanga khutu sangathe kumva? Kodi Iye amene anapanga diso sangathe kuona?
Onaj što uho zasadi da ne čuje? Koji stvori oko da ne vidi?
10 Kodi Iye amene amalangiza mitundu ya anthu sangathenso kulanga? Kodi Iye amene amaphunzitsa munthu angasowe nzeru?
Onaj što odgaja narode da ne kazni - Onaj što ljude uči mudrosti?
11 Yehova amadziwa maganizo a munthu; Iye amadziwa kuti maganizowo ndi achabechabe.
Jahve poznaje namisli ljudske: one su isprazne.
12 Wodala munthu amene Inu Yehova mumamulangiza, munthu amene mumamuphunzitsa kuchokera mulamulo lanu;
Blago onom koga ti poučavaš, Jahve, i učiš Zakonu svojemu:
13 mumamupumitsa pa nthawi ya mavuto, mpaka woyipa atakumbiridwa dzenje.
da mu mir udijeliš od nesretnih dana, dok se grob kopa zlikovcu.
14 Pakuti Yehova sadzawakana anthu ake; Iye sadzasiya cholowa chake.
Jer neće Jahve odbaciti naroda svojega i svoje baštine neće napustiti;
15 Chiweruzo chidzakhazikikanso pa chilungamo, ndipo onse olungama mtima adzachitsata.
jer će se pravo dosuditi pravednosti i za njom će ići svi čestiti srcem.
16 Ndani adzadzuka chifukwa cha ine kulimbana ndi anthu oyipa? Ndani adzayimirira mʼmalo mwanga kulimbana ndi anthu ochita zoyipa?
Tko će ustati za me protiv zlotvora? Tko će se zauzeti za me protiv zločinaca?
17 Yehova akanapanda kundithandiza, bwenzi nditakakhala msanga ku malo achete a imfa.
Da mi Jahve ne pomaže, brzo bih sišao u mjesto tišine.
18 Ndikanena kuti, “Phazi langa likuterereka,” chikondi chanu, Inu Yehova, chimandichirikiza.
Čim pomislim: “Noga mi posrće”, dobrota me tvoja, o Jahve, podupire.
19 Pamene nkhawa inakula mʼkati mwanga, chitonthozo chanu chinabweretsa chimwemwe mʼmoyo mwanga.
Kad se skupe tjeskobe u srcu mome, tvoje mi utjehe dušu vesele.
20 Kodi mpando waufumu woyipa ungathe kugwirizana nanu umene umabweretsa masautso chifukwa cha malamulo ake?
Zar je bezbožno sudište u savezu s tobom kad nevolje stvara pod izlikom zakona?
21 Iwo amasonkhana pamodzi kulimbana ndi wolungama ndi kugamula kuti wosalakwa aphedwe.
Nek' samo pritišću dušu pravednog, nek' osuđuju krv nedužnu:
22 Koma Yehova wakhala linga langa, ndipo Mulungu ndiye thanthwe limene ndimathawirako.
Jahve mi je utvrda, Bog - hrid utočišta moga.
23 Iye adzawabwezera chifukwa cha machimo awo ndi kuwawononga chifukwa cha kuyipa kwawo; Yehova Mulungu wathu adzawawononga.
Platit će im bezakonje njihovo, njihovom će ih zloćom istrijebiti, istrijebit će ih Jahve, Bog naš.

< Masalimo 94 >