< Masalimo 92 >

1 Salimo. Nyimbo ya pa tsiku la Sabata. Nʼkwabwino kutamanda Yehova ndi kuyimbira nyimbo dzina lanu, Inu Wammwambamwamba,
مزمور و سرود برای روز سبت خداوند را حمد گفتن نیکو است و به نام تو تسبیح خواندن، ای حضرت اعلی.۱
2 Kulengeza chikondi chanu mmawa, ndi kukhulupirika kwanu nthawi ya usiku,
بامدادان رحمت تو را اعلام نمودن و درهر شب امانت تو را.۲
3 kuyimbira nyimbo choyimbira cha zingwe khumi ndi mayimbidwe abwino a zeze.
بر ذات ده اوتار و بر رباب وبه نغمه هجایون و بربط.۳
4 Pakuti Inu mumandisangalatsa ndi ntchito zanu, Inu Yehova; Ine ndikuyimba mwachimwemwe pa ntchito ya manja anu.
زیرا که‌ای خداوند مرابه‌کارهای خودت شادمان ساخته‌ای. به‌سبب اعمال دستهای تو ترنم خواهم نمود.۴
5 Ndi yayikuludi ntchito yanu Yehova, maganizo anu ndi ozamadi!
‌ای خداوند اعمال تو چه عظیم است و فکرهای توبی نهایت عمیق.۵
6 Munthu wopanda nzeru sadziwa, zitsiru sizizindikira,
مرد وحشی این را نمی داند و جاهل در این تامل نمی کند.۶
7 kuti ngakhale anthu oyipa aphuka ngati udzu ndipo anthu onse ochita zoyipa apindula, adzawonongedwa kwamuyaya.
وقتی که شریران مثل علف می‌رویند و جمیع بدکاران می‌شکفند، برای این است که تا به ابد هلاک گردند.۷
8 Koma Inu Yehova, ndinu wokwezedwa kwamuyaya.
لیکن توای خداوند بر اعلی علیین هستی، تا ابدالاباد.۸
9 Zoonadi adani anu Yehova, zoonadi adani anu adzawonongeka; onse ochita zoyipa adzabalalitsidwa.
زیرا اینک دشمنان تو‌ای خداوند، هان دشمنان تو هلاک خواهند شد و جمیع بدکاران پراکنده خواهند شد.۹
10 Inu mwakweza nyanga yanga ngati nyanga ya njati; mafuta abwino akhuthulidwa pamutu wanga.
و اما شاخ مرا مثل شاخ گاو وحشی بلندکرده‌ای و به روغن تازه مسح شده‌ام.۱۰
11 Maso anga aona kugonjetsedwa kwa olimbana nane, makutu anga amva za kugwa kwa amaliwongo anga oyipa.
و چشم من بر دشمنانم خواهد نگریست و گوشهای من ازشریرانی که با من مقاومت می‌کنند خواهد شنید.۱۱
12 Anthu olungama adzaphuka ngati mtengo wa mgwalangwa, adzakula ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
عادل مثل درخت خرما خواهد شکفت و مثل سرو آزاد در لبنان نمو خواهد کرد.۱۲
13 odzalidwa mʼnyumba ya Yehova, adzakula bwino mʼmabwalo a Mulungu wathu.
آنانی که درخانه خداوند غرس شده‌اند، در صحنهای خدای ما خواهند شکفت.۱۳
14 Iwo adzaberekabe zipatso mu ukalamba wawo, adzakhala anthete ndi obiriwira,
در وقت پیری نیز میوه خواهند‌آورد و تر و تازه و سبز خواهند بود.۱۴
15 kulengeza kuti, “Yehova ndi wolungama; Iye ndiye Thanthwe langa, ndipo mwa Iye mulibe choyipa.”
تااعلام کنند که خداوند راست است. او صخره من است و در وی هیچ بی‌انصافی نیست.۱۵

< Masalimo 92 >