< Masalimo 92 >

1 Salimo. Nyimbo ya pa tsiku la Sabata. Nʼkwabwino kutamanda Yehova ndi kuyimbira nyimbo dzina lanu, Inu Wammwambamwamba,
Psalmus cantici, in die sabbati. [Bonum est confiteri Domino, et psallere nomini tuo, Altissime:
2 Kulengeza chikondi chanu mmawa, ndi kukhulupirika kwanu nthawi ya usiku,
ad annuntiandum mane misericordiam tuam, et veritatem tuam per noctem,
3 kuyimbira nyimbo choyimbira cha zingwe khumi ndi mayimbidwe abwino a zeze.
in decachordo, psalterio; cum cantico, in cithara.
4 Pakuti Inu mumandisangalatsa ndi ntchito zanu, Inu Yehova; Ine ndikuyimba mwachimwemwe pa ntchito ya manja anu.
Quia delectasti me, Domine, in factura tua; et in operibus manuum tuarum exsultabo.
5 Ndi yayikuludi ntchito yanu Yehova, maganizo anu ndi ozamadi!
Quam magnificata sunt opera tua, Domine! nimis profundæ factæ sunt cogitationes tuæ.
6 Munthu wopanda nzeru sadziwa, zitsiru sizizindikira,
Vir insipiens non cognoscet, et stultus non intelliget hæc.
7 kuti ngakhale anthu oyipa aphuka ngati udzu ndipo anthu onse ochita zoyipa apindula, adzawonongedwa kwamuyaya.
Cum exorti fuerint peccatores sicut fœnum, et apparuerint omnes qui operantur iniquitatem, ut intereant in sæculum sæculi:
8 Koma Inu Yehova, ndinu wokwezedwa kwamuyaya.
tu autem Altissimus in æternum, Domine.
9 Zoonadi adani anu Yehova, zoonadi adani anu adzawonongeka; onse ochita zoyipa adzabalalitsidwa.
Quoniam ecce inimici tui, Domine, quoniam ecce inimici tui peribunt; et dispergentur omnes qui operantur iniquitatem.
10 Inu mwakweza nyanga yanga ngati nyanga ya njati; mafuta abwino akhuthulidwa pamutu wanga.
Et exaltabitur sicut unicornis cornu meum, et senectus mea in misericordia uberi.
11 Maso anga aona kugonjetsedwa kwa olimbana nane, makutu anga amva za kugwa kwa amaliwongo anga oyipa.
Et despexit oculus meus inimicos meos, et in insurgentibus in me malignantibus audiet auris mea.
12 Anthu olungama adzaphuka ngati mtengo wa mgwalangwa, adzakula ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
Justus ut palma florebit; sicut cedrus Libani multiplicabitur.
13 odzalidwa mʼnyumba ya Yehova, adzakula bwino mʼmabwalo a Mulungu wathu.
Plantati in domo Domini, in atriis domus Dei nostri florebunt.
14 Iwo adzaberekabe zipatso mu ukalamba wawo, adzakhala anthete ndi obiriwira,
Adhuc multiplicabuntur in senecta uberi, et bene patientes erunt:
15 kulengeza kuti, “Yehova ndi wolungama; Iye ndiye Thanthwe langa, ndipo mwa Iye mulibe choyipa.”
ut annuntient quoniam rectus Dominus Deus noster, et non est iniquitas in eo.]

< Masalimo 92 >