< Masalimo 92 >

1 Salimo. Nyimbo ya pa tsiku la Sabata. Nʼkwabwino kutamanda Yehova ndi kuyimbira nyimbo dzina lanu, Inu Wammwambamwamba,
II est beau de louer l'Éternel, et de chanter à ton nom, ô Très-Haut!
2 Kulengeza chikondi chanu mmawa, ndi kukhulupirika kwanu nthawi ya usiku,
D'annoncer le matin ta bonté et ta fidélité durant les nuits;
3 kuyimbira nyimbo choyimbira cha zingwe khumi ndi mayimbidwe abwino a zeze.
Sur la lyre à dix cordes et sur le luth, au son des accords de la harpe!
4 Pakuti Inu mumandisangalatsa ndi ntchito zanu, Inu Yehova; Ine ndikuyimba mwachimwemwe pa ntchito ya manja anu.
Car, ô Éternel, tu m'as réjoui par tes œuvres; je me réjouirai des ouvrages de tes mains.
5 Ndi yayikuludi ntchito yanu Yehova, maganizo anu ndi ozamadi!
Que tes œuvres sont grandes, ô Éternel! tes pensées sont merveilleusement profondes!
6 Munthu wopanda nzeru sadziwa, zitsiru sizizindikira,
L'homme dépourvu de sens n'y connaît rien, et l'insensé ne comprend pas ceci:
7 kuti ngakhale anthu oyipa aphuka ngati udzu ndipo anthu onse ochita zoyipa apindula, adzawonongedwa kwamuyaya.
Que les méchants croissent comme l'herbe et que tous les ouvriers d'iniquité fleurissent, pour être détruits à jamais.
8 Koma Inu Yehova, ndinu wokwezedwa kwamuyaya.
Mais toi, Éternel, tu es élevé à toujours.
9 Zoonadi adani anu Yehova, zoonadi adani anu adzawonongeka; onse ochita zoyipa adzabalalitsidwa.
Car voici, tes ennemis, ô Éternel, car voici, tes ennemis périront; tous ceux qui pratiquent l'iniquité seront dispersés.
10 Inu mwakweza nyanga yanga ngati nyanga ya njati; mafuta abwino akhuthulidwa pamutu wanga.
Mais tu me fais lever la tête comme le buffle; je suis oint avec une huile fraîche.
11 Maso anga aona kugonjetsedwa kwa olimbana nane, makutu anga amva za kugwa kwa amaliwongo anga oyipa.
Et mon œil se plaît à regarder, mes oreilles à entendre ces méchants qui s'élèvent contre moi.
12 Anthu olungama adzaphuka ngati mtengo wa mgwalangwa, adzakula ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
Le juste croîtra comme le palmier; il s'élèvera comme le cèdre du Liban.
13 odzalidwa mʼnyumba ya Yehova, adzakula bwino mʼmabwalo a Mulungu wathu.
Plantés dans la maison de l'Éternel, ils fleuriront dans les parvis de notre Dieu.
14 Iwo adzaberekabe zipatso mu ukalamba wawo, adzakhala anthete ndi obiriwira,
Ils porteront encore des fruits dans la blanche vieillesse; ils seront vigoureux et verdoyants,
15 kulengeza kuti, “Yehova ndi wolungama; Iye ndiye Thanthwe langa, ndipo mwa Iye mulibe choyipa.”
Pour annoncer que l'Éternel est juste. Il est mon rocher, et il n'y a point d'injustice en lui.

< Masalimo 92 >