< Masalimo 92 >

1 Salimo. Nyimbo ya pa tsiku la Sabata. Nʼkwabwino kutamanda Yehova ndi kuyimbira nyimbo dzina lanu, Inu Wammwambamwamba,
A Psalm [or] Song for the sabbath day. [It is a] good [thing] to give thanks to the LORD, and to sing praises to thy name, O Most High.
2 Kulengeza chikondi chanu mmawa, ndi kukhulupirika kwanu nthawi ya usiku,
To show forth thy loving-kindness in the morning, and thy faithfulness every night.
3 kuyimbira nyimbo choyimbira cha zingwe khumi ndi mayimbidwe abwino a zeze.
Upon an instrument of ten strings, and upon the psaltery; upon the harp with a solemn sound.
4 Pakuti Inu mumandisangalatsa ndi ntchito zanu, Inu Yehova; Ine ndikuyimba mwachimwemwe pa ntchito ya manja anu.
For thou, LORD, hast made me glad through thy work: I will triumph in the works of thy hands.
5 Ndi yayikuludi ntchito yanu Yehova, maganizo anu ndi ozamadi!
O LORD, how great are thy works! [and] thy thoughts are very deep.
6 Munthu wopanda nzeru sadziwa, zitsiru sizizindikira,
A brutish man knoweth not; neither doth a fool understand this.
7 kuti ngakhale anthu oyipa aphuka ngati udzu ndipo anthu onse ochita zoyipa apindula, adzawonongedwa kwamuyaya.
When the wicked spring as the grass, and when all the workers of iniquity do flourish; [it is] that they shall be destroyed for ever:
8 Koma Inu Yehova, ndinu wokwezedwa kwamuyaya.
But thou, LORD, [art most] high for evermore.
9 Zoonadi adani anu Yehova, zoonadi adani anu adzawonongeka; onse ochita zoyipa adzabalalitsidwa.
For lo, thy enemies, O LORD, for lo, thy enemies shall perish; all the workers of iniquity shall be scattered.
10 Inu mwakweza nyanga yanga ngati nyanga ya njati; mafuta abwino akhuthulidwa pamutu wanga.
But my horn shalt thou exalt like [the horn of] an unicorn: I shall be anointed with fresh oil.
11 Maso anga aona kugonjetsedwa kwa olimbana nane, makutu anga amva za kugwa kwa amaliwongo anga oyipa.
My eye also shall see [my desire] on my enemies, [and] my ears shall hear [my desire] of the wicked that rise up against me.
12 Anthu olungama adzaphuka ngati mtengo wa mgwalangwa, adzakula ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
The righteous shall flourish like the palm-tree; he shall grow like a cedar in Lebanon.
13 odzalidwa mʼnyumba ya Yehova, adzakula bwino mʼmabwalo a Mulungu wathu.
Those that are planted in the house of the LORD shall flourish in the courts of our God.
14 Iwo adzaberekabe zipatso mu ukalamba wawo, adzakhala anthete ndi obiriwira,
They shall still bring forth fruit in old age; they shall be fat and flourishing;
15 kulengeza kuti, “Yehova ndi wolungama; Iye ndiye Thanthwe langa, ndipo mwa Iye mulibe choyipa.”
To show that the LORD [is] upright: [he is] my rock, and [there is] no unrighteousness in him.

< Masalimo 92 >