< Masalimo 92 >
1 Salimo. Nyimbo ya pa tsiku la Sabata. Nʼkwabwino kutamanda Yehova ndi kuyimbira nyimbo dzina lanu, Inu Wammwambamwamba,
“A psalm or song for the sabbath day.” It is a good thing to give thanks unto the Lord, and to sing praises unto thy name, O Most High:
2 Kulengeza chikondi chanu mmawa, ndi kukhulupirika kwanu nthawi ya usiku,
To tell in the morning of thy kindness, and of thy faithfulness in the nights.
3 kuyimbira nyimbo choyimbira cha zingwe khumi ndi mayimbidwe abwino a zeze.
Upon a ten-stringed instrument, and upon the psaltery; and with the sweet sound of the harp.
4 Pakuti Inu mumandisangalatsa ndi ntchito zanu, Inu Yehova; Ine ndikuyimba mwachimwemwe pa ntchito ya manja anu.
For thou hast caused me to rejoice, O Lord, through thy doing: because of the works of thy hands will I triumph.
5 Ndi yayikuludi ntchito yanu Yehova, maganizo anu ndi ozamadi!
How great are thy works, O Lord! exceedingly profound are thy thoughts.
6 Munthu wopanda nzeru sadziwa, zitsiru sizizindikira,
A brutish man knoweth it not, and a fool cannot understand this.
7 kuti ngakhale anthu oyipa aphuka ngati udzu ndipo anthu onse ochita zoyipa apindula, adzawonongedwa kwamuyaya.
When the wicked spring up like herbs, and when all the workers of wickedness do flourish; it is that they may be destroyed evermore.
8 Koma Inu Yehova, ndinu wokwezedwa kwamuyaya.
But thou art exalted to eternity, O Lord!
9 Zoonadi adani anu Yehova, zoonadi adani anu adzawonongeka; onse ochita zoyipa adzabalalitsidwa.
For, lo, thy enemies, O Lord, for, lo, thy enemies shall perish: all the workers of wickedness shall be scattered.
10 Inu mwakweza nyanga yanga ngati nyanga ya njati; mafuta abwino akhuthulidwa pamutu wanga.
But thou exaltest my horn like that of a reem: I am anointed with fresh oil.
11 Maso anga aona kugonjetsedwa kwa olimbana nane, makutu anga amva za kugwa kwa amaliwongo anga oyipa.
And my eye looketh on [the punishment of] those that regard me with envy: of the evildoers that rise up against me my ears shall bear it.
12 Anthu olungama adzaphuka ngati mtengo wa mgwalangwa, adzakula ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
The righteous shall spring up like the palm-tree: like a cedar in Lebanon shall he grow high.
13 odzalidwa mʼnyumba ya Yehova, adzakula bwino mʼmabwalo a Mulungu wathu.
Planted in the house of the Lord, in the courts of our God shall they spring up.
14 Iwo adzaberekabe zipatso mu ukalamba wawo, adzakhala anthete ndi obiriwira,
They shall still flourish in high old age; they shall be vigorous and covered with foliage;
15 kulengeza kuti, “Yehova ndi wolungama; Iye ndiye Thanthwe langa, ndipo mwa Iye mulibe choyipa.”
To declare that the Lord is upright: he is my rock, and there is no faultiness in him.