< Masalimo 92 >

1 Salimo. Nyimbo ya pa tsiku la Sabata. Nʼkwabwino kutamanda Yehova ndi kuyimbira nyimbo dzina lanu, Inu Wammwambamwamba,
A Psalm, a Song. For the sabbath day. It is a good thing to give thanks unto the LORD, and to sing praises unto Thy name, O Most High;
2 Kulengeza chikondi chanu mmawa, ndi kukhulupirika kwanu nthawi ya usiku,
To declare Thy lovingkindness in the morning, and Thy faithfulness in the night seasons,
3 kuyimbira nyimbo choyimbira cha zingwe khumi ndi mayimbidwe abwino a zeze.
With an instrument of ten strings, and with the psaltery; with a solemn sound upon the harp.
4 Pakuti Inu mumandisangalatsa ndi ntchito zanu, Inu Yehova; Ine ndikuyimba mwachimwemwe pa ntchito ya manja anu.
For Thou, LORD, hast made me glad through Thy work; I will exult in the works of Thy hands.
5 Ndi yayikuludi ntchito yanu Yehova, maganizo anu ndi ozamadi!
How great are Thy works, O LORD! Thy thoughts are very deep.
6 Munthu wopanda nzeru sadziwa, zitsiru sizizindikira,
A brutish man knoweth not, neither doth a fool understand this.
7 kuti ngakhale anthu oyipa aphuka ngati udzu ndipo anthu onse ochita zoyipa apindula, adzawonongedwa kwamuyaya.
When the wicked spring up as the grass, and when all the workers of iniquity do flourish; it is that they may be destroyed for ever.
8 Koma Inu Yehova, ndinu wokwezedwa kwamuyaya.
But Thou, O LORD, art on high for evermore.
9 Zoonadi adani anu Yehova, zoonadi adani anu adzawonongeka; onse ochita zoyipa adzabalalitsidwa.
For, lo, Thine enemies, O LORD, for, lo, Thine enemies shall perish: all the workers of iniquity shall be scattered.
10 Inu mwakweza nyanga yanga ngati nyanga ya njati; mafuta abwino akhuthulidwa pamutu wanga.
But my horn hast Thou exalted like the horn of the wild-ox; I am anointed with rich oil.
11 Maso anga aona kugonjetsedwa kwa olimbana nane, makutu anga amva za kugwa kwa amaliwongo anga oyipa.
Mine eye also hath gazed on them that lie in wait for me, mine ears have heard my desire of the evil-doers that rise up against me.
12 Anthu olungama adzaphuka ngati mtengo wa mgwalangwa, adzakula ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
The righteous shall flourish like the palm-tree; he shall grow like a cedar in Lebanon.
13 odzalidwa mʼnyumba ya Yehova, adzakula bwino mʼmabwalo a Mulungu wathu.
Planted in the house of the LORD, they shall flourish in the courts of our God.
14 Iwo adzaberekabe zipatso mu ukalamba wawo, adzakhala anthete ndi obiriwira,
They shall still bring forth fruit in old age; they shall be full of sap and richness;
15 kulengeza kuti, “Yehova ndi wolungama; Iye ndiye Thanthwe langa, ndipo mwa Iye mulibe choyipa.”
To declare that the LORD is upright, my Rock, in whom there is no unrighteousness.

< Masalimo 92 >