< Masalimo 92 >

1 Salimo. Nyimbo ya pa tsiku la Sabata. Nʼkwabwino kutamanda Yehova ndi kuyimbira nyimbo dzina lanu, Inu Wammwambamwamba,
A Canticle Psalm. On the day of the Sabbath. It is good to confess to the Lord and to sing psalms to your name, O Most High:
2 Kulengeza chikondi chanu mmawa, ndi kukhulupirika kwanu nthawi ya usiku,
to announce your mercy in the morning, and your truth throughout the night,
3 kuyimbira nyimbo choyimbira cha zingwe khumi ndi mayimbidwe abwino a zeze.
upon the ten strings, upon the psaltery, with a canticle, upon stringed instruments.
4 Pakuti Inu mumandisangalatsa ndi ntchito zanu, Inu Yehova; Ine ndikuyimba mwachimwemwe pa ntchito ya manja anu.
For you, O Lord, have delighted me with your doings, and I will exult in the works of your hands.
5 Ndi yayikuludi ntchito yanu Yehova, maganizo anu ndi ozamadi!
How great are your works, O Lord! Your thoughts have been made exceedingly deep.
6 Munthu wopanda nzeru sadziwa, zitsiru sizizindikira,
A foolish man will not know these things, and a senseless one will not understand:
7 kuti ngakhale anthu oyipa aphuka ngati udzu ndipo anthu onse ochita zoyipa apindula, adzawonongedwa kwamuyaya.
when sinners will have risen up like grass, and when all those who work iniquity will have appeared, that they shall pass away, age after age.
8 Koma Inu Yehova, ndinu wokwezedwa kwamuyaya.
But you, O Lord, are the Most High for all eternity.
9 Zoonadi adani anu Yehova, zoonadi adani anu adzawonongeka; onse ochita zoyipa adzabalalitsidwa.
For behold your enemies, O Lord, for behold your enemies will perish, and all those who work iniquity will be dispersed.
10 Inu mwakweza nyanga yanga ngati nyanga ya njati; mafuta abwino akhuthulidwa pamutu wanga.
And my horn will be exalted like that of the single-horned beast, and my old age will be exalted in fruitful mercy.
11 Maso anga aona kugonjetsedwa kwa olimbana nane, makutu anga amva za kugwa kwa amaliwongo anga oyipa.
And my eye has looked down upon my enemies, and my ear will hear of the malignant rising up against me.
12 Anthu olungama adzaphuka ngati mtengo wa mgwalangwa, adzakula ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
The just one will flourish like the palm tree. He will be multiplied like the cedar of Lebanon.
13 odzalidwa mʼnyumba ya Yehova, adzakula bwino mʼmabwalo a Mulungu wathu.
Those planted in the house of the Lord will flourish in the courts of the house of our God.
14 Iwo adzaberekabe zipatso mu ukalamba wawo, adzakhala anthete ndi obiriwira,
They will still be multiplied in a fruitful old age, and they will endure well,
15 kulengeza kuti, “Yehova ndi wolungama; Iye ndiye Thanthwe langa, ndipo mwa Iye mulibe choyipa.”
so that they may announce that the Lord our God is righteous and that there is no iniquity in him.

< Masalimo 92 >