< Masalimo 92 >

1 Salimo. Nyimbo ya pa tsiku la Sabata. Nʼkwabwino kutamanda Yehova ndi kuyimbira nyimbo dzina lanu, Inu Wammwambamwamba,
It is a good thing to give thanks to Jehovah, and to sing praises to thy name, O Most High,
2 Kulengeza chikondi chanu mmawa, ndi kukhulupirika kwanu nthawi ya usiku,
to show forth thy loving kindness in the morning, and thy faithfulness every night,
3 kuyimbira nyimbo choyimbira cha zingwe khumi ndi mayimbidwe abwino a zeze.
with an instrument of ten strings, and with the psaltery, with a solemn sound upon the harp.
4 Pakuti Inu mumandisangalatsa ndi ntchito zanu, Inu Yehova; Ine ndikuyimba mwachimwemwe pa ntchito ya manja anu.
For thou, Jehovah, have made me glad through thy work. I will triumph in the works of thy hands.
5 Ndi yayikuludi ntchito yanu Yehova, maganizo anu ndi ozamadi!
How great are thy works, O Jehovah! Thy thoughts are very deep.
6 Munthu wopanda nzeru sadziwa, zitsiru sizizindikira,
A brutish man knows not, nor does a fool understand this.
7 kuti ngakhale anthu oyipa aphuka ngati udzu ndipo anthu onse ochita zoyipa apindula, adzawonongedwa kwamuyaya.
When the wicked spring as the grass, and when all the workers of iniquity flourish, it is that they shall be destroyed forever,
8 Koma Inu Yehova, ndinu wokwezedwa kwamuyaya.
but thou, O Jehovah, are on high for evermore.
9 Zoonadi adani anu Yehova, zoonadi adani anu adzawonongeka; onse ochita zoyipa adzabalalitsidwa.
For, lo, thine enemies, O Jehovah, for, lo, thine enemies shall perish. All the workers of iniquity shall be scattered.
10 Inu mwakweza nyanga yanga ngati nyanga ya njati; mafuta abwino akhuthulidwa pamutu wanga.
But thou have exalted my horn like the wild ox's. I am anointed with fresh oil,
11 Maso anga aona kugonjetsedwa kwa olimbana nane, makutu anga amva za kugwa kwa amaliwongo anga oyipa.
and my eye has seen my enemies. My ears have heard of the evildoers who rise up against me.
12 Anthu olungama adzaphuka ngati mtengo wa mgwalangwa, adzakula ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
A righteous man shall flourish like the palm tree. He shall grow like a cedar in Lebanon.
13 odzalidwa mʼnyumba ya Yehova, adzakula bwino mʼmabwalo a Mulungu wathu.
Men who are planted in the house of Jehovah shall flourish in the courts of our God.
14 Iwo adzaberekabe zipatso mu ukalamba wawo, adzakhala anthete ndi obiriwira,
They shall still bring forth fruit in old age. They shall be full of sap and green
15 kulengeza kuti, “Yehova ndi wolungama; Iye ndiye Thanthwe langa, ndipo mwa Iye mulibe choyipa.”
to show that Jehovah is upright. He is my rock, and there is no unrighteousness in him.

< Masalimo 92 >