< Masalimo 92 >

1 Salimo. Nyimbo ya pa tsiku la Sabata. Nʼkwabwino kutamanda Yehova ndi kuyimbira nyimbo dzina lanu, Inu Wammwambamwamba,
En Salme. En Sang for Sabbatsdagen.
2 Kulengeza chikondi chanu mmawa, ndi kukhulupirika kwanu nthawi ya usiku,
Det er godt at takke HERREN, lovsynge dit Navn, du Højeste,
3 kuyimbira nyimbo choyimbira cha zingwe khumi ndi mayimbidwe abwino a zeze.
ved Gry forkynde din Naade, om Natten din Trofasthed
4 Pakuti Inu mumandisangalatsa ndi ntchito zanu, Inu Yehova; Ine ndikuyimba mwachimwemwe pa ntchito ya manja anu.
til tistrenget Lyre, til Harpe, til Strengeleg paa Citer!
5 Ndi yayikuludi ntchito yanu Yehova, maganizo anu ndi ozamadi!
Thi ved dit Værk har du glædet mig, HERRE, jeg jubler over dine Hænders Gerning.
6 Munthu wopanda nzeru sadziwa, zitsiru sizizindikira,
Hvor store er dine Gerninger, HERRE, dine Tanker saare dybe!
7 kuti ngakhale anthu oyipa aphuka ngati udzu ndipo anthu onse ochita zoyipa apindula, adzawonongedwa kwamuyaya.
Taaben fatter det ikke, Daaren skønner ej sligt.
8 Koma Inu Yehova, ndinu wokwezedwa kwamuyaya.
Spirer de gudløse end som Græsset, blomstrer end alle Udaadsmænd, er det kun for at lægges øde for stedse,
9 Zoonadi adani anu Yehova, zoonadi adani anu adzawonongeka; onse ochita zoyipa adzabalalitsidwa.
men du er ophøjet for evigt, HERRE.
10 Inu mwakweza nyanga yanga ngati nyanga ya njati; mafuta abwino akhuthulidwa pamutu wanga.
Thi se, dine Fjender, HERRE, se, dine Fjender gaar under, alle Udaadsmænd spredes!
11 Maso anga aona kugonjetsedwa kwa olimbana nane, makutu anga amva za kugwa kwa amaliwongo anga oyipa.
Du har løftet mit Horn som Vildoksens, kvæget mig med den friskeste Olie;
12 Anthu olungama adzaphuka ngati mtengo wa mgwalangwa, adzakula ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
det fryder mit Øje at se mine Fjender, mit Øre at høre mine Avindsmænd.
13 odzalidwa mʼnyumba ya Yehova, adzakula bwino mʼmabwalo a Mulungu wathu.
De retfærdige grønnes som Palmen, vokser som Libanons Ceder;
14 Iwo adzaberekabe zipatso mu ukalamba wawo, adzakhala anthete ndi obiriwira,
plantet i HERRENS Hus grønnes de i vor Guds Forgaarde;
15 kulengeza kuti, “Yehova ndi wolungama; Iye ndiye Thanthwe langa, ndipo mwa Iye mulibe choyipa.”
selv graanende bærer de Frugt, er friske og fulde af Saft for at vidne, at HERREN er retvis, min Klippe, hos hvem ingen Uret findes.

< Masalimo 92 >