< Masalimo 92 >

1 Salimo. Nyimbo ya pa tsiku la Sabata. Nʼkwabwino kutamanda Yehova ndi kuyimbira nyimbo dzina lanu, Inu Wammwambamwamba,
Žalm a píseň, ke dni sobotnímu. Dobré jest oslavovati Hospodina, a žalmy zpívati jménu tvému, ó Nejvyšší,
2 Kulengeza chikondi chanu mmawa, ndi kukhulupirika kwanu nthawi ya usiku,
Zvěstovati každé jitro milosrdenství tvé, a pravdu tvou každé noci,
3 kuyimbira nyimbo choyimbira cha zingwe khumi ndi mayimbidwe abwino a zeze.
Při nástroji o desíti strunách, při loutně, a při harfě s písničkou.
4 Pakuti Inu mumandisangalatsa ndi ntchito zanu, Inu Yehova; Ine ndikuyimba mwachimwemwe pa ntchito ya manja anu.
Nebo jsi mne rozveselil, Hospodine, skutky svými, o skutcích rukou tvých zpívati budu.
5 Ndi yayikuludi ntchito yanu Yehova, maganizo anu ndi ozamadi!
Jak velicí jsou skutkové tvoji, Hospodine! Velmi hluboká jsou myšlení tvá.
6 Munthu wopanda nzeru sadziwa, zitsiru sizizindikira,
Èlověk hovadný nezná toho, aniž blázen rozumí tomu,
7 kuti ngakhale anthu oyipa aphuka ngati udzu ndipo anthu onse ochita zoyipa apindula, adzawonongedwa kwamuyaya.
Že vyrostají bezbožní jako bylina, a kvetou všickni činitelé nepravosti, aby vyhlazeni byli na věky.
8 Koma Inu Yehova, ndinu wokwezedwa kwamuyaya.
Ty pak, ó Nejvyšší, že na věky jsi Hospodin.
9 Zoonadi adani anu Yehova, zoonadi adani anu adzawonongeka; onse ochita zoyipa adzabalalitsidwa.
Nebo aj, nepřátelé tvoji, Hospodine, nebo aj, nepřátelé tvoji zahynou; rozptýleni budou všickni činitelé nepravosti.
10 Inu mwakweza nyanga yanga ngati nyanga ya njati; mafuta abwino akhuthulidwa pamutu wanga.
Můj pak roh vyzdvihneš jako jednorožcův, pokropen budu olejem novým.
11 Maso anga aona kugonjetsedwa kwa olimbana nane, makutu anga amva za kugwa kwa amaliwongo anga oyipa.
I podívá se oko mé na ty, jenž mne špehují, a o těch nešlechetnících, jenž proti mně povstávají, ušima svýma uslyším.
12 Anthu olungama adzaphuka ngati mtengo wa mgwalangwa, adzakula ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
Spravedlivý jako palma kvésti bude, a jako cedr na Libánu rozloží se.
13 odzalidwa mʼnyumba ya Yehova, adzakula bwino mʼmabwalo a Mulungu wathu.
Štípení v domě Hospodinově v síňcích Boha našeho kvésti budou.
14 Iwo adzaberekabe zipatso mu ukalamba wawo, adzakhala anthete ndi obiriwira,
Ještě i v šedinách ovoce ponesou, spanilí a zelení budou,
15 kulengeza kuti, “Yehova ndi wolungama; Iye ndiye Thanthwe langa, ndipo mwa Iye mulibe choyipa.”
Aby to zvěstováno bylo, že přímý jest Hospodin, skála má, a že nepravosti žádné při něm není.

< Masalimo 92 >